< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Tako so ti trije možje prenehali odgovarjati Jobu, ker je bil pravičen v svojih lastnih očeh.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
Potem je bil vžgan bes Elihúja, Barahélovega sina, Buzéjca iz Rámovega rodu. Njegov bes je bil vžgan zoper Joba, ker je sebe bolj opravičeval kakor Boga.
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
Tudi zoper njegove tri prijatelje je bil vžgan njegov bes, ker niso našli nobenega odgovora, pa so vendar obsodili Joba.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Torej Elihú je čakal, dokler Job ni spregovoril, ker so bili starejši kakor on.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
Ko je Elihú videl, da ni bilo nobenega odgovora v ustih teh treh mož, je bil potem vžgan njegov bes.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
Elihú, Barahélov sin, Buzéjec, je odgovoril in rekel: »Jaz sem mlad, vi pa ste zelo stari, zato sem bil prestrašen in se vam nisem drznil pokazati svojega mnenja.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Rekel sem: ›Dnevi naj bi spregovorili in množica let naj bi učila modrost.‹
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Toda v človeku je duh. Navdih Vsemogočnega jim daje razumevanje.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Veliki možje niso vedno modri niti ostareli ne razumejo sodbe.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Zato sem rekel: ›Prisluhnite mi. Tudi jaz bom pokazal svoje mnenje.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Glejte, čakal sem na vaše besede, prisluhnil sem vašim razlogom, medtem ko ste iskali, kaj bi rekli.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Da, prisluhnil sem vam in glejte nikogar izmed vas ni bilo, da prepriča Joba ali da odgovori njegovim besedam,
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
da ne bi rekli: ›Pridobili smo modrost. Bog ga suva dol, ne človek.‹
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Torej svojih besed ni usmeril zoper mene niti mu ne bom odgovoril z vašimi govori.«
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Bili so osupli, niso več odgovarjali. Prenehali so govoriti.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Ko sem čakal (kajti niso govorili, temveč mirno stali in niso več odgovarjali),
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
sem rekel: »Tudi jaz bom odgovoril svoj del, tudi jaz bom pokazal svoje mišljenje.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
Kajti poln sem stvari, duh znotraj mene me sili.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Glejte, moj trebuh je kakor vino, ki nima oddušnika. Pripravljeno je, da poči kakor novi mehovi.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Govoril bom, da bom lahko osvežen. Odprl bom svoje ustnice in odgovoril.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Ne pustite mi, prosim vas, sprejeti obličja kateregakoli moža niti mi ne pustite, da dajem laskave nazive človeku.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
Kajti ne znam dajati laskavih nazivov. Če bi tako počel, bi me moj stvarnik hitro odvedel.

< Yobu 32 >