< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Тада престаше она три човека одговарати Јову, јер се чињаше да је праведан.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
А Елијуј, син Варахилов од Вуза, рода Рамовог, разгневи се на Јова што се сам грађаше праведнији од Бога;
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
И на три пријатеља његова разгневи се што не нађоше одговора и опет осуђиваху Јова.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Јер Елијуј чекаше докле они говораху с Јовом, јер беху старији од њега.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
Па кад виде Елијуј да нема одговора у устима она три човека, распали се гнев његов.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
И проговори Елијуј син Варахилов од Вуза, и рече: Ја сам најмлађи, а ви сте старци, зато се бојах и не смех вам казати шта мислим.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Мишљах: нека говори старост, и многе године нека објаве мудрост.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Али је дух у људима, и Дух Свемогућег уразумљује их.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Велики нису свагда мудри, и старци не знају свагда шта је право.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Зато велим: послушај ме да кажем и ја како мислим.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Ето, чекао сам да ви изговорите, слушао сам разлоге ваше докле извиђасте беседу.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Пазио сам, али гле, ни један од вас не сапре Јова, не одговори на његове речи.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Може бити да ћете рећи: Нађосмо мудрост, Бог ће га оборити, не човек.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Није на ме управио беседе, ни ја му нећу одговарати вашим речима.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Смели су се, не одговарају више, нестало им је речи.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Чекао сам, али не говоре, стадоше, и више не одговарају.
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Одговорићу и ја за се, казаћу и ја како мислим.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
Јер сам пун речи, тесно је духу у мени.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Гле, трбух је мој као вино без одушке, и распукао би се као нов мех.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Говорићу да одахнем, отворићу усне своје, и одговорићу.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Нећу гледати ко је ко, и човеку ћу говорити без ласкања.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
Јер не умем ласкати; одмах би ме узео Творац мој.

< Yobu 32 >