< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Когда те три мужа перестали отвечать Иову, потому что он был прав в глазах своих,
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
тогда воспылал гнев Елиуя, сына Варахиилова, Вузитянина из племени Рамова: воспылал гнев его на Иова за то, что он оправдывал себя больше, нежели Бога,
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
а на трех друзей его воспылал гнев его за то, что они не нашли, что отвечать, а между тем обвиняли Иова.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Елиуй ждал, пока Иов говорил, потому что они летами были старше его.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
Когда же Елиуй увидел, что нет ответа в устах тех трех мужей, тогда воспылал гнев его.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
И отвечал Елиуй, сын Варахиилов, Вузитянин, и сказал: я молод летами, а вы - старцы; поэтому я робел и боялся объявлять вам мое мнение.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Я говорил сам себе: пусть говорят дни, и многолетие поучает мудрости.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Но дух в человеке и дыхание Вседержителя дает ему разумение.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Не многолетние только мудры, и не старики разумеют правду.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Поэтому я говорю: выслушайте меня, объявлю вам мое мнение и я.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Вот, я ожидал слов ваших, - вслушивался в суждения ваши, доколе вы придумывали, что сказать.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Я пристально смотрел на вас, и вот никто из вас не обличает Иова и не отвечает на слова его.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Не скажите: мы нашли мудрость: Бог опровергнет его, а не человек.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Если бы он обращал слова свои ко мне, то я не вашими речами отвечал бы ему.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Испугались, не отвечают более; перестали говорить.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
И как я ждал, а они не говорят, остановились и не отвечают более,
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
то и я отвечу с моей стороны, объявлю мое мнение и я,
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
ибо я полон речами, и дух во мне теснит меня.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Вот, утроба моя, как вино неоткрытое: она готова прорваться, подобно новым мехам.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Поговорю, и будет легче мне; открою уста мои и отвечу.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
На лице человека смотреть не буду и никакому человеку льстить не стану,
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
потому что я не умею льстить: сейчас убей меня, Творец мой.

< Yobu 32 >