< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Então aquelles tres homens cessaram de responder a Job; porque era justo aos seus proprios olhos.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
E accendeu-se a ira d'Elihu, filho de Baracheel o buzita, da familia de Ram: contra Job se accendeu a sua ira, porque se justificava a si mesmo, mais do que a Deus.
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
Tambem a sua ira se accendeu contra os seus tres amigos: porque, não achando que responder, todavia condemnavam a Job.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Elihu porém esperou que Job fallasse; porquanto tinham mais edade do que elle.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
Vendo pois Elihu que já não havia resposta na bocca d'aquelles tres homens, a sua ira se accendeu.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
E respondeu Elihu, filho de Baracheel o buzita, e disse: Eu sou de menos edade, e vós sois edosos; receei-me e temi de vos declarar a minha opinião.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Dizia eu: Fallem os dias, e a multidão doa annos ensine a sabedoria.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Na verdade, ha um espirito no homem, e a inspiração do Todo-poderoso os faz entendidos.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Os grandes não são os sabios, nem os velhos entendem juizo.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Pelo que digo: Dae-me ouvidos, e tambem eu declararei a minha opinião.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Eis que aguardei as vossas palavras, e dei ouvidos ás vossas considerações, até que buscasseis razões.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Attentando pois para vós, eis que nenhum de vós ha que possa convencer a Job, nem que responda ás suas razões:
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Para que não digaes: Achamos a sabedoria; Deus o derribou, e não homem algum.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Ora elle não dirigiu contra mim palavra alguma, nem lhe responderei com as vossas palavras.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Estão pasmados, não respondem mais, faltam-lhes as palavras.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Esperei pois, porém não fallam: porque já pararam, e não respondem mais.
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Tambem eu responderei pela minha parte: tambem eu declararei a minha opinião.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
Porque estou cheio de palavras, e aperta-me o espirito do meu ventre.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Eis que o meu ventre é como o mosto, sem respiradouro, e virá a arrebentar, como odres novos.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Fallarei, e respirarei: abrirei os meus labios, e responderei.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Oxalá eu não faça accepção de pessoas, nem use de sobrenomes com o homem!
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
Porque não sei usar de sobrenomes: em breve me levaria o meu Creador.

< Yobu 32 >