< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Dei tri mennerne svara ikkje Job meir, av di han heldt seg sjølv for rettferdig.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
Men då loga harmen upp hjå Elihu, son åt Barak’el, buziten, av Rams-ætti. Han vart harm på Job, av di han heldt seg sjølv rettferdigare enn Gud.
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
Han harmast og på dei tri venerne, av di dei ikkje kunde finna noko svar, og endå dømde Job skuldig.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
For Elihu hadde venta med å tala til Job, av di dei andre var eldre enn han;
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
men då Elihu såg at dei tri mennerne ikkje hadde noko å svara, vart han brennande harm.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
Og Elihu, son åt Barak’el, buziten, tok til ords og sagde: «Ung er eg etter år å rekna; de derimot er gamle menn. Difor eg blygdest og var rædd å segja til dykk det eg veit.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Eg tenkte: «Åri tala lyt og alderen forkynna visdom.»
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Nei, ånd lyt til hjå menneski; og Allvalds ande gjev deim vit.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Dei gamle er’kje alltid vise, kvithærde veit’kje stødt det rette.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Difor eg segjer: Høyr på meg; eg vil og segja det eg veit.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Eg venta hev på dykkar ord og lydde vel på dykkar lærdom, alt med de leita etter ord.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Og eg gav nøgje agt på dykk, men ingen sagde Job imot, ingen av dykk gav honom svar.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Seg ikkje: «Visdom der me fann; Gud slå han ned, folk kann det ikkje.»
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Han hev’kje tala imot meg, og ei med dykkar ord eg svarar.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Dei er forstøkte, svarar ikkje, dei vantar ord å føra fram.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Treng eg vel venta når dei tegjer og stend der reint forutan svar?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Eg vil og svara, eg for meg, eg vil og segja det eg veit.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
For eg er full av ord til svars; i bringa sprengjer åndi på.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Mitt indre er som innstengd vin, lik nye vinhit vil det sprengjast.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Eg tala vil so eg fær luft, vil opna lipporne og svara.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Eg ikkje tek parti for nokon og smeikjer ei for nokor mann;
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
å smeikja kann eg ikkje med; min skapar elles burt meg reiv.

< Yobu 32 >