< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
De tre menn svarte ikke Job mere, fordi han var rettferdig i sine egne øine.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
Da optendtes Elihus vrede - han stammet fra Bus og var sønn av Barak'el, av Rams ætt. Mot Job optendtes hans vrede, fordi han holdt sig selv for å være rettferdig for Gud,
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
og mot hans tre venner optendtes hans vrede, fordi de ikke fant noget svar og allikevel dømte Job skyldig.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Elihu hadde ventet med å tale til Job, fordi de andre var eldre av år enn han.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
Da nu Elihu så at det ikke var noget svar i de tre menns munn, da optendtes hans vrede.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
Så tok da Elihu, sønn av Barak'el, busitten, til orde og sa: Jeg er ung av år, og I er gråhårede; derfor holdt jeg mig tilbake og torde ikke uttale for eder hvad jeg vet.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Jeg tenkte: La alderen tale og de mange år forkynne visdom!
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Dog, det er menneskets ånd og den Allmektiges åndepust som gjør forstandig.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
De gamle er ikke alltid vise, ikke alltid forstår oldinger hvad rett er.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Derfor sier jeg: Hør nu på mig! Også jeg vil uttale hvad jeg vet.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Jeg ventet på eders ord, jeg lyttet efter forstandig tale fra eder, mens I grundet på hvad I skulde si.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Jeg gav akt på eder; men det var ingen av eder som gjendrev Job, ingen som svarte på hans ord.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Si ikke: Vi har funnet visdom hos ham; bare Gud kan få bukt med ham, ikke noget menneske!
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Han har jo ikke rettet sin tale mot mig, og med eders ord vil jeg ikke svare ham.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
De er forferdet og svarer ikke mere; ordene er blitt borte for dem.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Skal jeg vente, fordi de ikke taler, fordi de står der og ikke svarer mere?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Også jeg vil nu svare for min del; også jeg vil uttale hvad jeg vet.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
For jeg er full av ord; ånden i mitt indre driver mig.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Mitt indre er som innestengt vin; som nyfylte skinnsekker vil det revne.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Jeg vil tale, så jeg kan få luft; jeg vil åpne mine leber og svare.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Jeg vil ikke ta parti for nogen, og jeg vil ikke smigre for noget menneske;
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
for jeg forstår ikke å smigre; ellers kunde min skaper lett rykke mig bort.

< Yobu 32 >