< Yobu 32 >
1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Forsothe these thre men leften of to answere Joob, for he semyde a iust man to hem.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
And Helyu, the sone of Barachel Buzites, of the kynrede of Ram, was wrooth, and hadde indignacioun; forsothe he was wrooth ayens Joob, for he seide hym silf to be iust bifor God.
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
Sotheli Helyu hadde indignacioun ayens the thre frendis of hym, for thei hadden not founde resonable answere, but oneli hadde condempned Joob.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Therfor Helyu abood Joob spekynge, for thei, that spaken, weren eldere men.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
But whanne he hadde seyn, that thre men myyten not answere, he was wrooth greetly.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
And Helyu, the sone of Barachel Buzites, answeride, and seyde, Y am yongere in tyme, sotheli ye ben eldere; therfor with heed holdun doun Y dredde to schewe to you my sentence.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
For Y hopide that lengere age schulde speke, and that the multitude of yeeris schulden teche wisdom.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
But as Y se, spirit is in men, and the enspiryng `ether reuelacioun, of Almyyti God yyueth vndurstondyng.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Men of long lijf ben not wise, and elde men vndurstonden not doom.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Therfor Y schal seie, Here ye me, and Y also schal schewe my kunnyng to you.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
For Y abood youre wordis, Y herde youre prudence, as long as ye dispuytiden in youre wordis.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
And as long as Y gesside you to seie ony thing, Y bihelde; but as Y se, `noon is of you, that may repreue Joob, and answere to hise wordis;
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
lest perauenture ye seien, We han founde wisdom; God, and not man, hath cast hym awei.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Joob spak no thing to me, and Y not bi youre wordis schal answere hym.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Thei dredden, and answeriden no more, and token awei speche fro hem silf.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Therfor for Y abood, and thei spaken not, thei stoden, and answeriden no more; also Y schal answere my part,
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
and Y schal schewe my kunnyng.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
For Y am ful of wordis, and the spirit of my wombe, `that is, mynde, constreyneth me.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Lo! my wombe is as must with out `spigot, ether a ventyng, that brekith newe vessels.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Y schal speke, and brethe ayen a litil; Y schal opene my lippis, and Y schal answere.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Y schal not take the persoone of man, and Y schal not make God euene to man.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
For Y woot not hou long Y schal abide, and if my Makere take me awei `after a litil tyme.