< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
So these three men ceased to answer Job, because he was righteous in his own eyes.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
Then was kindled the wrath of Elihu the son of Barachel the Buzite, of the family of Ram: against Job was his wrath kindled, because he justified himself rather than God.
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
Also against his three friends was his wrath kindled, because they had found no answer, and yet had condemned Job.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Now Elihu had waited to speak unto Job, because they were elder than he.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
And when Elihu saw that there was no answer in the mouth of these three men, his wrath was kindled.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
And Elihu the son of Barachel the Buzite answered and said, I am young, and ye are very old; wherefore I held back, and durst not shew you mine opinion.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
I said, Days should speak, and multitude of years should teach wisdom.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
But there is a spirit in man, and the breath of the Almighty giveth them understanding.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
It is not the great that are wise, nor the aged that understand judgment.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Therefore I said, Hearken to me; I also will shew mine opinion.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Behold, I waited for your words, I listened for your reasons, whilst ye searched out what to say.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Yea, I attended unto you, and, behold, there was none that convinced Job, or that answered his words, among you.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Beware lest ye say, We have found wisdom; God may vanquish him, not man:
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
For he hath not directed his words against me; neither will I answer him with your speeches.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
They are amazed, they answer no more: they have not a word to say.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
And shall I wait, because they speak not, because they stand still, and answer no more?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
I also will answer my part, I also will shew mine opinion.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
For I am full of words; the spirit within me constraineth me.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Behold, my belly is as wine which hath no vent; like new bottles it is ready to burst.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
I will speak, that I may be refreshed; I will open my lips and answer.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Let me not, I pray you, respect any man’s person; neither will I give flattering titles unto any man.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
For I know not to give flattering titles; [else] would my Maker soon take me away.

< Yobu 32 >