< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
So had these three men abstained from answering Job; because he was righteous in his own eyes.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
Thereupon was kindled the wrath of Elihu the son of Barachel the Buzite, of the family of Ram: against Job was his wrath kindled, because he had declared himself more righteous than God.
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
And against his three friends was his wrath kindled; because they had found no answer, and yet had condemned Job.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Now Elihu had held back toward Job [his] words; because the others were older in days than he.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
But when Elihu saw that there was no answer in the mouth of these three men, then was his wrath kindled.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
And Elihu the son of Barachel the Buzite commenced, and said, Young am I in days, and ye are very old: therefore I hesitated and feared to show you what I know.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
I had said, Days shall speak, and multitude of years shall make wisdom known.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
But it is the spirit in man, and the breath of the Almighty which giveth them understanding.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Not those rich in years must be always wise: neither do the aged constantly understand what is just.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Therefore do I say, Hearken to me: I also will show forth what I know myself.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Behold, I waited for your words: I gave an attentive ear to your reasonings, till you might have searched out the [proper] words.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
And now I understand you fully, and, behold, there is none that convinceth Job, or, that answereth his speeches among you.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Say then not, We have found wisdom: God will thrust him down, not man.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
But he hath not directed any words against me: and with your speeches will I not answer him.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
They are dismayed, they answer no more: words have escaped away from them.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
And should I wait [longer], because they cannot speak, because they stand stilt and answer no more?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
[But] I also will surely answer my part, I myself also will show forth what I know;
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
For I am full of words, the spirit in my bosom urgeth me hard.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Behold, my bosom is like [fresh] wine which hath not been opened: like new bottles it is ready to burst.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
I will speak, that I may breathe freer: I will open my lips and answer.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
On no account will I show undue favor to any man, and to no son of earth will I give flattering titles.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
For I know not to give flattering titles; [for else] my Maker would speedily carry me away.

< Yobu 32 >