< Yobu 32 >
1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
And these three men ceased to answer Job, because he was righteous in his own eyes.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
Then was kindled the anger of Elihu the son of Barachel, the Buzite, of the family of Ram: against Job was his anger kindled, because he justified himself rather than God;
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
and against his three friends was his anger kindled, because they found no answer, and [yet] condemned Job.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
But Elihu had waited till Job had finished speaking, because they were older than he.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
And Elihu saw that there was no answer in the mouth of the three men, and his anger was kindled.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
And Elihu the son of Barachel the Buzite answered and said, I am young, and ye are aged; wherefore I was timid, and feared to shew you what I know.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
I said, Let days speak, and multitude of years teach wisdom.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
But there is a spirit which is in man; and the breath of the Almighty giveth them understanding.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
It is not the great that are wise; neither do the aged understand judgment.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Therefore I say, Hearken to me; I also will shew what I know.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Lo, I waited for your words; I gave ear to your reasonings, until ye searched out what to say.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Yea, I gave you mine attention, and behold, there was none of you that confuted Job, that answered his words;
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
That ye may not say, We have found out wisdom; God will make him yield, not man.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Now he hath not directed [his] words against me; and I will not answer him with your speeches. ...
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
They were amazed, they answered no more; words failed them.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
And I waited, for they spoke not, but stood still, and answered no more; —
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
I will answer, I also in my turn, I also will shew what I know:
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
For I am full of matter, the spirit within me constraineth me.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Behold, my belly is as wine which hath no vent; like new flasks, it is ready to burst.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
I will speak, that I may find relief; I will open my lips and answer.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Let me not, I pray you, accept any man's person; neither will I give flattery to man.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
For I know not how to flatter; my Maker would soon take me away.