< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Da nu hine tre Mænd ikke mere svarede Job, fordi han var retfærdig i sine egne Øjne,
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
blussede Vreden op i Buziten Elihu, Barak'els Søn, af Rams Slægt. Paa Job vrededes han, fordi han gjorde sig retfærdigere end Gud,
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
og paa hans tre Venner, fordi de ikke fandt noget Svar og dog dømte Job skyldig.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Elihu havde ventet, saa længe de talte med Job, fordi de var ældre end han;
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
men da han saa, at de tre Mænd intet havde at svare, blussede hans Vrede op;
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
og Buziten Elihu, Barak'els Søn, tog til Orde og sagde: Ung af Dage er jeg, og I er gamle Mænd, derfor holdt jeg mig tilbage, angst for at meddele eder min Viden;
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
jeg tænkte: »Lad Alderen tale og Aarenes Mængde kundgøre Visdom!«
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Dog Aanden, den er i Mennesket, og den Almægtiges Aande giver dem Indsigt;
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
de gamle er ikke altid de kloge, Oldinge ved ej altid, hvad Ret er;
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
derfor siger jeg: Hør mig, lad ogsaa mig komme frem med min Viden!
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Jeg biede paa, at I skulde tale, lyttede efter forstandige Ord, at I skulde finde de rette Ord;
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
jeg agtede nøje paa eder; men ingen af eder gendrev Job og gav Svar paa hans Ord.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Sig nu ikke: »Vi stødte paa Visdom, Gud maa fælde ham, ikke et Menneske!«
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Mod mig har han ikke rettet sin Tale, og med eders Ord vil jeg ikke svare ham.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
De blev bange, svarer ej mer, for dem slap Ordene op.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Skal jeg tøve, fordi de tier og staar der uden at svare et Ord?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Ogsaa jeg vil svare min Del, ogsaa jeg vil frem med min Viden!
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
Thi jeg er fuld af Ord, Aanden i mit Bryst trænger paa;
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
som tilbundet Vin er mit Bryst, som nyfyldte Vinsække nær ved at sprænges;
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
tale vil jeg for at faa Luft, aabne mine Læber og svare.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Forskel gør jeg ikke og smigrer ikke for nogen;
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
thi at smigre bruger jeg ikke, snart rev min Skaber mig ellers bort!

< Yobu 32 >