< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
“Me ne mʼani yɛɛ apam sɛ meremfi akɔnnɔ mu, nhwɛ ababaa.
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Dɛn ne onipa kyɛfa a efi ɔsoro Nyankopɔn nkyɛn? Dɛn ne nʼagyapade a efi ɔsoro Tumfo no nkyɛn?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Ɛnyɛ ɔsɛe mma amumɔyɛfo, atoyerɛnkyɛm mma wɔn a wɔyɛ bɔne ana?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Onhu mʼakwan na ɔnkan anammɔn biara a mitu ana?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
“Sɛ manantew wɔ nkontompo mu anaasɛ matu mmirika adi nnaadaasɛm akyi a,
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
ma Onyankopɔn nkari me wɔ nsania papa so na obehu sɛ me ho nni asɛm;
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
sɛ mʼanammɔntu afom ɔkwan, sɛ me koma adi mʼani akyi, anaasɛ me nsa ho agu fi a
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
ɛno de ma afoforo nni nea madua, na ma wontutu me nnɔbae ngu.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
“Sɛ ɔbea bi atɔ me koma so, anaasɛ matɛw me yɔnko bi pon akyi a,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
ɛno de, me yere nyam ɔbarima foforo aduan, na mmarima afoforo ne no nna.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
Efisɛ anka ɛno na ɛbɛyɛ aniwusɛm ne bɔne a ɛsɛ sɛ wɔtwe aso wɔ so.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
Ɛyɛ ogya a ɛhyew kodu Ɔsɛe mu; na ebetumi atutu me nnɔbae ase.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
“Sɛ mabu mʼasomfo mmarima ne mmea ntɛnkyew, bere a wɔne me nyaa asɛm,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
sɛ Onyankopɔn de si mʼanim a dɛn na mɛyɛ? Sɛ wɔfrɛ me akontaabu a, mmuae bɛn na mɛma?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Ɛnyɛ nea ɔbɔɔ me wɔ ɔyafunu mu no na ɔbɔɔ wɔn? Ɛnyɛ onipa koro no na ɔyɛɛ yɛn baanu wɔ yɛn nanom yafunu mu?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
“Sɛ mamma ahiafo nea wɔn koma pɛ anaa mama akunafo ani ayɛ wɔn yaw,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
sɛ mabɔ mʼaduan ho atirimɔden a mamma ayisaa bi,
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
nanso efi mmerantebere mu matetew no sɛnea agya bɛyɛ, na efi ɔyafunu mu, mahwɛ akunafo.
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
Sɛ mahu obi a onni adurade na ɔrebrɛ, anaa ohiani bi a onni atade,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
na sɛ wɔamfi koma mu anhyira me sɛ mede me nguan ho nwi kaa wɔn hyew,
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
sɛ mama me nsa so atia ayisaa bi, esiane sɛ mewɔ tumi wɔ asennii nti a,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
ɛno de, ma me basa mpan mfi me mmati, ma emmubu mfi nʼapɔw so.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
Misuroo ɔsɛe a efi Onyankopɔn nkyɛn, na nʼanuonyam ho suro nti mantumi anyɛ saa nneyɛe no.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
“Sɛ mede me werɛ ahyɛ sikakɔkɔɔ mu anaasɛ maka akyerɛ sikakɔkɔɔ ankasa se, ‘Wo na wobɔ me ho ban,’
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
sɛ masɛpɛw me ho wɔ mʼahode bebrebe nti, ahode a me nsa aka yi,
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
sɛ mahwɛ owia ne ne hyerɛn anaa ɔsram a ɔnam anuonyam mu,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
ama aka me koma a obiara nnim na me nsa yɛɛ wɔn atuu de nidi maa wɔn a,
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
ɛno de, na eyinom nso bɛyɛ bɔne a wobu ho atɛn, efisɛ na manni Onyankopɔn a ɔte ɔsoro no nokware.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
“Sɛ mʼani gyee wɔ me tamfo amanehunu nti anaa mesrew no wɔ ɔhaw a aba ne so nti,
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
memmaa mʼano nyɛɛ bɔne sɛ mɛdome ne nkwa,
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
sɛ nnipa a wɔwɔ me fi mu nkaa da sɛ, ‘Hena na Hiob pon so nam mmee no da?’
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
Ɔhɔho biara anna abɔnten so da, efisɛ me pon ano daa hɔ da biara maa akwantufo,
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
Makata me bɔne so sɛnea nnipa yɛ de mʼafɔdi ahyɛ me koma mu
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
esiane sɛ misuroo nnipadɔm ne ahohora a efi mmusua hɔ no nti na meyɛɛ komm a mamfi adi.
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
(“Ao, sɛ anka mewɔ obi a obetie me. Mede me din ahyɛ mʼanoyi ase, ma Otumfo no mmua me; ma nea ɔbɔ me kwaadu no nkyerɛw ne sobobɔ.
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Ampa ara, mɛhyɛ wɔ me mmati, mɛhyɛ sɛ ahenkyɛw.
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
Mebu mʼanammɔntu biara ho akontaa akyerɛ no; mɛkɔ nʼanim sɛ ɔheneba.)
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
“Sɛ mʼasase teɛ mu tia me na nusu fɔw ne nkɔ nyinaa,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
sɛ madi so aba a mintuaa ka anaasɛ mabu so apaafo no aba mu a,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
ma nsɔe mfifi nsi awi anan mu na wura mfuw nsi atoko anan mu.” Hiob nsɛm no asi.

< Yobu 31 >