< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
En pakt hadde jeg gjort med mine øine, at jeg ikke skulde se på en jomfru.
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Hvad lodd vilde jeg ellers få av Gud i himmelen, eller hvad arv av den Allmektige i det høie?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Rammer ikke fordervelse den urettferdige, og ulykke dem som gjør det onde?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Ser ikke han mine veier, og teller han ikke alle mine skritt?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Dersom jeg har faret frem med falskhet, og min fot har hastet til svik
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
- la Gud veie mig på rettferds vektskål, og han skal se at jeg er uten skyld -
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
dersom mine skritt har bøid av fra veien, og mitt hjerte har fulgt mine øine, og dersom der er nogen flekk på mine hender,
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
gid da en annen må ete det jeg har sådd, og gid det jeg har plantet, må rykkes op med rot!
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
Dersom mitt hjerte har latt sig dåre for en kvinnes skyld, og jeg har luret ved min næstes dør,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
gid da min hustru må male korn for en annen, og andre menn bøie sig over henne!
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
For slikt er en skjenselsdåd, det er en misgjerning, hjemfalt til dom;
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
det er en ild som fortærer like til avgrunnen; alt mitt gods skulde den gjøre ende på.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
Har jeg krenket min træls og min trælkvinnes rett, når de hadde nogen trette med mig?
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
Hvad skulde jeg da gjøre om Gud stod op, og hvad skulde jeg svare ham om han gransket saken?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Har ikke han som skapte mig i mors liv, skapt også dem, og har ikke en og den samme dannet oss i mors liv?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
Har jeg nektet fattigfolk det de ønsket, og latt enkens øine tæres bort?
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
Har jeg ett mitt brød alene, så den farløse ikke fikk ete av det?
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
Nei, fra min ungdom av vokste han op hos mig som hos en far, og fra min mors liv av førte jeg henne ved hånden.
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
Har jeg kunnet se en ulykkelig uten klær eller en fattig uten et plagg å ha på sig?
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
Måtte ikke hans lender velsigne mig, fordi han fikk varme sig med ull av mine får?
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
Har jeg løftet min hånd mot den farløse, fordi jeg var viss på å få medhold i retten?
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
Gid da min skulder må falle fra sitt ledd, og min arm bli brutt løs fra sin skål!
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
For Guds straff fylte mig med redsel, og mot hans velde maktet jeg intet.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
Har jeg satt mitt håp til gullet og sagt til gullklumpen: Du er min tillit?
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
Har jeg gledet mig fordi min rikdom blev stor, og fordi min hånd vant mig meget gods?
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
Når jeg så sollyset, hvorledes det strålte, og månen, hvor herlig den skred frem,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
blev da mitt hjerte dåret i lønndom, så jeg sendte dem håndkyss?
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
Nei, også det vilde være en misgjerning, hjemfalt til dom; for da hadde jeg fornektet Gud i det høie.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
Har jeg gledet mig ved min fiendes uferd og jublet når ulykken rammet ham?
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
Nei, jeg tillot ikke min munn å synde ved å forbanne ham og ønske ham døden.
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
Må ikke mine husfolk vidne at enhver fikk mette sig ved mitt bord?
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
Aldri måtte en fremmed ligge utenfor mitt hus om natten; jeg åpnet mine dører for den veifarende.
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
Har jeg, som mennesker pleier, skjult mine synder og dulgt min misgjerning i min barm,
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
fordi jeg fryktet den store mengde og var redd for de fornemme slekters forakt, så jeg tidde stille og ikke gikk ut av min dør?
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Å, om jeg hadde nogen som vilde høre på mig! Se, her er min underskrift, la den Allmektige svare mig! Å, om jeg hadde det skrift min motpart har satt op!
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Sannelig, jeg skulde ta det på min skulder, jeg skulde feste det til mitt hode som en krone;
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
jeg skulde gjøre ham regnskap for alle mine skritt, som en fyrste skulde jeg møte ham.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
Dersom min aker skriker over mig, og alle dens furer gråter,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
dersom jeg har fortæret dens grøde uten betaling og utslukket dens eiers liv,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
gid det da må vokse torner på min aker istedenfor hvete og ugress istedenfor bygg! Her ender Jobs ord.

< Yobu 31 >