< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Ngenza isivumelwano lamehlo ami; pho ngingananzelela njani intombi?
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Ngoba siyini isabelo sikaNkulunkulu esivela phezulu, lelifa likaSomandla elivela endaweni eziphezulu?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Incithakalo kayisiyomubi yini, lengozi yabenzi bobubi?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Yena kaziboni yini indlela zami, abale zonke izinyathelo zami?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Uba ngihambe ngokuyize, kumbe unyawo lwami luphuthumele enkohlisweni,
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
kangilinganise ngesilinganiso esilungileyo, ukuze uNkulunkulu azi ubuqotho bami.
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
Uba inyathelo lami liphambukile endleleni, lenhliziyo yami yalandela amehlo ami, kumbe kunamathele isici ezandleni zami;
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
kangihlanyele, kodwa kudle omunye, lezilimo zami zisitshulwe.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
Uba inhliziyo yami iyengwe ngowesifazana, kumbe ngacathama emnyango kamakhelwane wami,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
umkami kacholele omunye, labanye kabaguqe phezu kwakhe.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
Ngoba lokho kuyinkohlakalo, njalo kuyisono ngabahluleli.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
Ngoba ngumlilo odla kuze kube yincithakalo, usiphule sonke isivuno sami.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
Uba ngalile udaba lwenceku yami loba olwencekukazi yami, lapho ziphikisana lami,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
pho ngizakwenzani lapho uNkulunkulu esukuma? Lalapho esethekela, ngizaphendulani kuye?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Lowo owangenza esiswini kamenzanga yena yini, lowasibumba esiswini munye?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
Uba ngigodlele umyanga isifiso, kumbe ngifiphaze amehlo omfelokazi,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
kumbe ngadla ucezu lwami ngedwa, ukuze intandane ingadli kulo
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
(ngoba kwasebutsheni bami yakhula lami nginjengoyise, ngamqondisa kusukela esizalweni sikamama),
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
uba ngabona obhubha ngenxa yokuswela isigqoko, loba umyanga engelasembatho,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
uba inkalo zakhe zingangibusisanga, ngoba ekhudunyezwe yiboya bezimvu zami,
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
uba ngaphakamisa isandla sami ngimelene lentandane, lapho ngabona usizo lwami esangweni,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
kaliwe ihlombe lami esiphangeni sami, lengalo yami iqamuke ethanjeni layo.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
Ngoba incithakalo kaNkulunkulu yayiyisesabiso kimi, ngingenelisi ngenxa yobukhulu bakhe.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
Uba ngenzile igolide laba lithemba lami, ngathi kugolide elihle: Themba lami.
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
Uba ngithokozile ngoba inotho yami inengi, langoba isandla sami sithole okunengi;
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
uba ngikhangele ilanga lapho libenyezela, loba inyanga ehamba enkazimulweni,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
lenhliziyo yami yayengwa ensitha, kumbe isandla sami sange umlomo wami,
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
lalokho yisiphambeko phambi kwabehluleli, ngoba ngabe ngimphikile uNkulunkulu waphezulu.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
Uba ngithokozile ngokuchitheka kongizondayo, kumbe ngajabula lapho ububi bumthola;
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
njalo ngingavumelanga umlomo wami ukuthi wone, ngokucela umphefumulo wakhe ngesiqalekiso;
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
uba abantu bethente lami bebengatshongo ukuthi: Hawu, aluba besilokwenyama yakhe, ngabe kasisuthanga.
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
Owemzini kazanga alale esitaladeni; iminyango yami ngayivulela isihambi.
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
Uba ngasibekela iziphambeko zami njengoAdamu, ngokufihla isono sami esifubeni sami.
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
Ngoba ngethuswa lixuku elikhulu, lokudelelwa ngabensendo kwangesabisa, ngakho ngathula, kangaze ngaphuma emnyango.
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Kungathi ngabe ngilongangizwa! Khangelani uphawu lwami. Kungathi uSomandla angangiphendula, lokuthi ophikisana lami ngabe ubhale ugwalo!
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Isibili, bengingaluthwala ehlombe lami, ngilubophe lube ngumqhele kimi.
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
Ngimtshele inani lezinyathelo zami, ngisondele kuye njengesiphathamandla.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
Uba umhlaba wami ukhalile ngami, lemifolo yawo ililile ndawonye,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
uba ngidlile amandla awo kungelamali, kumbe ngenza umphefumulo wabaniniwo uphele,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
kakuhlume ukhula oluhlabayo endaweni yengqoloyi, lokhula olunukayo endaweni yebhali. Amazwi kaJobe asephelile.

< Yobu 31 >