< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Szövetséget kötöttem szemeimmel, hogyan vetnék hát ügyet hajadonra?
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Hisz mely osztályrész jut Istentől felülről s mely örökség a Mindenhatótól a magasból?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Nemde balsors a jogtalannak s viszontagság a gonosztevőknek.
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Nemde ő látja útaimat s mind a lépéseimet megszámlálja!
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Ha hamissággal jártam és csalárdságra sietett a lábam –
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
mérjen meg engem igaz serpenyőn s tudja meg Isten gáncstalanságomat –
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
ha léptem elhajolt az útról és szemeim után járt a szívem, kezeimhez hiba tapadt:
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
hadd vessek és más egyék, és sarjaim tépessenek ki gyökerestül!
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
Ha szívem elcsábíttatta magát asszony miatt, felebarátom ajtaján leskelődtem:
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
másnak őröljön a feleségem és mások hajoljanak reá;
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
mert gazság az, s bírák elé való bűn az,
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
mert tűz az, mely az enyészetig emészt, s minden termésemet gyökerestül tépi ki!
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
Ha megvetettem szolgám és szolgálóm jogát, mikor pöröltek velem –
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
hiszen mit teszek majd, midőn Isten fölkel s midőn számon kér, mit felelek neki,
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
hiszen az anyaméhben ki engem alkotott, alkotta őt és Egy formált minket a méhben –
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
ha megvontam a kívántat a szegényektől s az özvegy szemeit epesztettem,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
s én egyedül ettem falatomat s árva nem evett belőle
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
– hisz ifjúkorom óta nálam nőtt fel, mint atyánál, s mint anyám méhéből valót úgy vezettem -;
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
ha láttam bujdosót öltözet nélkül s takarója nincs a szűkölködőnek,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
ha nem áldottak engem ágyékai s bárányaim nyíretéből fel nem melegedett;
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
ha fölemeltem kezemet az árvára, midőn a kapuban láttam segítségemet:
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
vállam essék ki a lapoczkájából és törjék el karom a szárából;
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
mert rettenet nekem az Istentől való balsors, s fensége miatt nem tehetném!
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
Ha aranyat tettem bizalmammá és a színaranyat mondtam bizodalmamnak;
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
ha örültem, hogy nagy a vagyonom s hogy sokat ért el kezem;
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
ha láttam a napvilágot, hogy ragyog, s a holdat, a mint dicsőn halad,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
és szívem elcsábult titokban és kezem csókra nyúlt a szájamhoz:
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
az is bíró elé való bűn, mert megtagadtam volna Istent felülről!
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
Ha örültem gyűlölőm elesésén s felbuzdultam, midőn baj érte –
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
hisz nem engedtem ínyemet, hogy vétkezzen, hogy átokkal kérjem lelkét -;
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
ha nem mondták sátram emberei: bár volna, ki húsából nem lakott jól
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
az utczán nem hált meg jövevény, az út felé tártam ki ajtaimat -;
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
ha emberek módjára takargattam bűntetteimet, keblemre rejtve bűnömet,
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
mert rettegtem a nagy tömegtől s megijesztett a családok gúnyja, úgy hogy csendben voltam, nem mentem ki a kapun!
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Vajha volna, ki rám hallgatna – íme jegyem, feleljen nekem a Mindenható – és a vádlevél, melyet írt a pörös felem:
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
bizony, vállamon hordanám azt, felfűzném koszorúnak magamra,
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
lépéseim számát bevallanám neki, akár egy fejedelem közeledném hozzá!
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
Ha ellenem kiáltott földem s egyaránt sírtak barázdái;
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
ha erejét emésztettem pénz nélkül és gazdájával kileheltettem lelkét:
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
búza helyett sarjadjon bogáncs, és árpa helyett gazfű! Vége Jób beszédeinek.

< Yobu 31 >