< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
“I made a covenant with my eyes; how then should I look lustfully at a young woman?
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
For what is the portion from God above, and the heritage from the Almighty on high?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Is it not calamity to the unrighteous, and disaster to the workers of iniquity?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Doesn’t he see my ways, and count all my steps?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
“If I have walked with falsehood, and my foot has hurried to deceit
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
(let me be weighed in an even balance, that God may know my integrity);
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
if my step has turned out of the way, if my heart walked after my eyes, if any defilement has stuck to my hands,
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
then let me sow, and let another eat. Yes, let the produce of my field be rooted out.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
“If my heart has been enticed to a woman, and I have laid wait at my neighbour’s door,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
then let my wife grind for another, and let others sleep with her.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
For that would be a heinous crime. Yes, it would be an iniquity to be punished by the judges,
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
for it is a fire that consumes to destruction, and would root out all my increase.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
“If I have despised the cause of my male servant or of my female servant, when they contended with me,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
what then will I do when God rises up? When he visits, what will I answer him?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Didn’t he who made me in the womb make him? Didn’t one fashion us in the womb?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
“If I have withheld the poor from their desire, or have caused the eyes of the widow to fail,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
or have eaten my morsel alone, and the fatherless has not eaten of it
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
(no, from my youth he grew up with me as with a father, I have guided her from my mother’s womb);
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
if I have seen any perish for want of clothing, or that the needy had no covering;
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
if his heart hasn’t blessed me, if he hasn’t been warmed with my sheep’s fleece;
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
if I have lifted up my hand against the fatherless, because I saw my help in the gate;
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
then let my shoulder fall from the shoulder blade, and my arm be broken from the bone.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
For calamity from God is a terror to me. Because of his majesty, I can do nothing.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
“If I have made gold my hope, and have said to the fine gold, ‘You are my confidence;’
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
If I have rejoiced because my wealth was great, and because my hand had gotten much;
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
if I have seen the sun when it shined, or the moon moving in splendour,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
and my heart has been secretly enticed, and my hand threw a kiss from my mouth;
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
this also would be an iniquity to be punished by the judges, for I would have denied the God who is above.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
“If I have rejoiced at the destruction of him who hated me, or lifted up myself when evil found him
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
(I have certainly not allowed my mouth to sin by asking his life with a curse);
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
if the men of my tent have not said, ‘Who can find one who has not been filled with his meat?’
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
(the foreigner has not camped in the street, but I have opened my doors to the traveller);
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
if like Adam I have covered my transgressions, by hiding my iniquity in my heart,
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
because I feared the great multitude, and the contempt of families terrified me, so that I kept silence, and didn’t go out of the door—
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
oh that I had one to hear me! Behold, here is my signature! Let the Almighty answer me! Let the accuser write my indictment!
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Surely I would carry it on my shoulder, and I would bind it to me as a crown.
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
I would declare to him the number of my steps. I would go near to him like a prince.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
If my land cries out against me, and its furrows weep together;
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
if I have eaten its fruits without money, or have caused its owners to lose their life,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
let briers grow instead of wheat, and stinkweed instead of barley.” The words of Job are ended.

< Yobu 31 >