< Yobu 31 >
1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
A covenant I made to eyes my and what? will I look carefully on a virgin.
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
And what? - [is] [the] portion of God above and [the] inheritance of [the] Almighty from high places.
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
¿ Not [does] calamity [belong] to an evil-doer and misfortune to [those who] do wickedness.
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
¿ Not he does he see ways my and all steps my does he count?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
If I have walked with falsehood and it has made haste to deceit foot my.
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
Let him weigh me in balances of righteousness and let him acknowledge God integrity my.
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
If it turned aside step my from the way and after eyes my it has gone heart my and to hands my it has stuck a blemish.
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
Let me sow and another let him eat and produce my let them be rooted up.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
If it has been deceived heart my on a woman and at [the] doorway of neighbor my I have lain in wait.
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
Let her grind for another wife my and over her let them bow down! others.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
For (that *Q(K)*) [is] wickedness (and that *Q(k)*) [is] iniquity judges.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
For [is] a fire that [which] to Abaddon it will devour and all produce my it will root up.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
If I rejected [the] cause of male servant my and female servant my in complaint their with me.
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
And what? will I do if he will arise God and if he will visit what? will I respond to him.
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
¿ Not in the belly [the one who] made me did he make him and did prepare us? he in the womb one.
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
If I withheld any of [the] desire of poor [people] and [the] eyes of a widow I caused to fail.
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
And I may eat morsel of bread my to alone me and not he ate a fatherless one some of it.
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
For since youth my he grew up with me like a father and from [the] womb of mother my I guided her.
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
If I saw [one who] was perishing because not clothing and not covering [belonged] to the needy [person].
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
If not they blessed me (loins his *Q(K)*) and from [the] fleece of lambs my he warmed himself.
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
If I brandished on a fatherless one hand my for I saw in the gate help my.
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
Shoulder my from its shoulder let it fall and arm my from arm its let it be broken.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
For [was] a fear to me calamity of God and from majesty his not I am able.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
If I have made gold confidence my and to pure gold I have said security my.
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
If I rejoiced for [was] great wealth my and for much it had found hand my.
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
If I saw a light that it shone and [the] moon splendid [was] going.
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
And it was gullible in secrecy heart my and it kissed hand my mouth my.
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
Also that [is] iniquity calling for judgment for I denied God above.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
If I rejoiced in [the] disaster of [one who] hated me and I excited myself if it had found him calamity.
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
And not I have permitted to sin palate my by asking for by a curse life his.
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
If not they have said [the] men of tent my who? will he give from meat his not [one who] is satisfied.
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
In the street not he passed [the] night a sojourner doors my to the path I opened.
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
If I have concealed like Adam transgressions my by hiding in bosom my iniquity my.
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
For I feared - a multitude great and [the] contempt of clans it caused to be dismayed me and I was silent not I went outside [the] door.
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Who? will he give [will belong] to me - [one who] listens to me here! mark my [the] Almighty let him answer me and a document [which] he had written [the] person of case my.
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
If not on shoulder my I will carry it I will tie on it a crown to myself.
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
[the] number of Steps my I will tell to him like a chief I will approach him.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
If on me land my it cried out and together furrows its they wept!
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
If produce its I have eaten not money and [the] life of owners its I have caused to breathe out.
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
In place of wheat - let it come forth thorn[s] and in place of barley foul weed[s] they are finished [the] words of Job.