< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Jeg sluttede en Pagt med mit Øje om ikke at se på en Jomfru;
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
hvad var ellers min Lod fra Gud hist oppe, den Arv, den Almægtige gav fra det høje?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Har ikke den lovløse Vanheld i Vente, Udådsmændene Modgang?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Ser han ej mine Veje og tæller alle mine Skridt?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Har jeg holdt til med Løgn, og hasted min Fod til Svig
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
på Rettens Vægtskål veje han mig, så Gud kan kende min Uskyld
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
er mit Skridt bøjet af fra Vejen, og har mit Hjerte fulgt mine Øjne, hang noget ved mine Hænder,
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
da gid jeg må så og en anden fortære, og hvad jeg planted, oprykkes med Rode!
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
Blev jeg en Dåre på Grund at en Kvinde, og har jeg luret ved Næstens Dør,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
så dreje min Hustru Kværn for en anden, og andre bøje sig over hende!
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
Thi sligt var Skændselsdåd, Brøde, der drages for Retten,
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
ja, Ild, der æder til Afgrunden og sætter hele min Høst i Brand!
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
Har jeg ringeagtet min Træls og min Trælkvindes Ret, når de trættede med mig,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
hvad skulde jeg da gøre, når Gud stod op, hvad skulde jeg svare, når han så efter?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Har ikke min Skaber skabt ham i Moders Skød, har en og samme ej dannet os begge i Moders Liv?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
Har jeg afslået ringes Ønske, ladet Enkens Øjne vansmægte,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
var jeg ene om at spise mit Brød, har den faderløse ej spist deraf
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
nej, fra Barnsben fostred jeg ham som en Fader, jeg ledede hende fra min Moders Skød.
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
Har jeg set en Stakkel blottet for Klæder, en fattig savne et Tæppe
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
visselig nej, hans Hofter velsigned mig, når han varmed sig i Uld af mine Lam.
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
Har jeg løftet min Bånd mod en faderløs, fordi jeg var vis på Medhold i Retten,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
så falde min Skulder fra Nakken, så rykkes min Arm af Led!
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
Thi Guds Rædsel var kommet over mig, og når han rejste sig, magted jeg intet!
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
Har jeg slået min Lid til Guld, kaldt det rene Guld min Fortrøstning,
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
var det min Glæde, at Rigdommen voksed, og at min Hånd fik sanket så meget,
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
så jeg, hvorledes Sollyset stråled, eller den herligt skridende Måne,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
og lod mit Hjerte sig dåre i Løn, så jeg hylded dem med Kys på min Hånd
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
også det var Brøde, der drages for Retten, thi da fornægted jeg Gud hist oppe.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
Var min Avindsmands Fald min Glæd jubled jeg, når han ramtes af Vanheld
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
nej, jeg tillod ikke min Gane at synde, så jeg bandende kræved hans Sjæl.
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
Har min Husfælle ej måttet sige: "Hvem mættedes ej af Kød fra hans Bord"
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
nej, den fremmede lå ej ude om Natten, jeg åbned min Dør for Vandringsmænd.
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
Har jeg skjult mine Synder, som Mennesker gør, så jeg dulgte min Brøde i Brystet
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
af Frygt for den store Hob, af Angst for Stamfrænders Ringeagt, så jeg blev inden Døre i Stilhed!
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Ak, var der dog en, der hørte på mig! Her er mit Bomærke - lad den Almægtige svare! Havde jeg blot min Modparts Indlæg!
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Sandelig, tog jeg det på min Skulder, kransed mit Hoved dermed som en Krone,
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
svared ham for hvert eneste Skridt og mødte ham som en Fyrste.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
Har min Mark måttet skrige over mig og alle Furerne græde,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
har jeg tæret dens Kraft uden Vederlag, udslukt dens Ejeres Liv,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
så gro der Tjørn for Hvede og Ukrudt i Stedet for Byg! Her ender Jobs Ord.

< Yobu 31 >