< Yobu 31 >
1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Paipi te ka mik neh ka saii dongah me tlam lae oila te ka yakming eh?
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
A so lamkah Pathen khoyo neh hmuensang lamkah Tlungthang rho te menim?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Boethae ham rhainah neh boethae aka saii ham yoethaenah moenih a?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Amah loh ka longpuei a hmuh tih ka khokan boeih he a tae moenih a?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
A poeyoek taengah ka pongpa tih ka kho loh a hlangthai palat taengla a tawn uh atah,
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
Duengnah cooi dongah kai n'khiing saeh lamtah Pathen loh ka muelhtuetnah ming saeh.
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
Longpuei lamloh ka khokan a buung atah, ka mik hnukah ka lungbuei cet tih ka kut dongah a lolhmaih a kap atah,
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
ka soem vaengah a tloe loh ca saeh lamtah ka cadil rhoek te ha uh saeh.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
Huta loh ka lungbuei a hlae tih ka hui kah thohka ah ka rhongngol atah,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
Ka yuu loh a tloe la kuelh saeh lamtah a taengah hlang tloe bakop mai saeh.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
Te dongah te khonuen rhamtat neh te te thaesainah rhokhan ni.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
Te hmai loh Abaddon duela a hlawp tih ka cangvuei te boeih ha.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
Ka salpa neh ka salnu loh kai taengah a tuituk vaengah tiktamnah ka hnawt atah,
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
Pathen a thoh vaengah balae ka saii vetih n'hip vaengah amah te metlam ol ka mael eh?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Bungko khuiah kai aka saii loh anih a saii moenih a? Kaimih he bung khuiah pakhat la n'cuen sak.
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
tattloel kah kongaih te ka hloh pah tih nuhmai mik te ka khah sak koinih,
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
Kamah buhkam te kamah bueng loh ka caak tih cadah loh ca pawt koinih,
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
Ka camoe lamloh napa bangla ka taengah pantai tih nuhmai khaw a nu bung lamloh ka mawt.
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
Pueinak mueh tih himbai tling la aka milh khodaeng te ka hmuh mai tih,
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
A pumpu, a pumpu ah kai n'uem uh vaengah ka tu mul neh ka hlung pawt mai koinih,
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
Vongka ah kai bomkung te ka hmuh vaengah ka kut he cadah soah ka ka thueng atah,
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
ka laengpang he a hnuk lamloh rhul saeh lamtah ka ban a cung dong lamloh tlawt mai saeh.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
Pathen taengkah rhainah te kai ham ka birhihnah la a om dongah a boeimangnah te ka noeng moenih.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
Sui te ka uepnah la ka khueh tih sui cilh te ka pangtungnah la ka thui koinih,
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
Ka thadueng len tih ka kut loh a khuet la a hmuh dongah ka kokhahnah atah,
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
Vangnah dongah a thangthen tih hla vang a thoeih te ka hmuh vaengah,
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
ka lungbuei he yinhnuk ah hloih tih ka kut loh ka ka te mok koinih.
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
He khaw a so kah Pathen taengah ka basa la om vetih thaesainah lai la om ni.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
Ka lunguet kah yoethaenah dongah ka kohoe tih yoethae loh anih taengla a thoeng te ka haenghang puei atah,
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
A hinglu te thaephoeinah neh hoe hamla ka ka he laihmu la ka khueh aih moenih.
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
Ka dap kah hlang rhoek loh, “U long nim a maeh te a cung pawt la a paek eh?” a ti uh moenih a?
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
Ka thohkhaih kah yinlai te caehlong ka ong pah tih vongvoel ah a rhaeh moenih.
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
Hlang bangla ka boekoeknah ka dah tih, kai kathaesainah he ka thindang ah ka det mai akhaw,
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
hlangping te yet taengah ka sarhing tih huiko kah nueihbu loh kai n'rhihyawp sak. Te dongah ka kuemsuem tih thohka la ka moe pawh.
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Kai taengkah aka hnatun la kamah taengah u long nim m'paek lah mako? Ka kutha he Tlungthang loh kai n'doo saeh lamtah ka tuituknah he hlang loh cabu la daek saeh.
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Te te ka laengpang ah ka koh vetih te te ka soah rhuisam la ka laikoeinah het mahpawt nim?
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
Ka khokan tarhing la a taengah ka puen lah vetih anih te rhaengsang bangla ka paan lah mako.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
Ka khohmuen loh kai m'pang thil tih a kong te rhenten rhap koinih,
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
A thadueng te tangka mueh la ka caak tih a kungmah kah hinglu ka yawn sak atah,
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
Cang yueng la mutlo hling, cangtun yueng la saeldol khaw poe saeh,” a ti. Job kah ol bawt coeng.