< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
А тепер насміхаються з мене молодші від мене літами, ті, що їхніх батьків я бриди́вся б покласти із псами отари моєї.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Та й сила рук їхніх для чого бува́ла мені? Повня сил їх мину́лась!
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Само́тні були в недоста́тку та голоді, ссали вони суху землю, зруйновану та опустілу!
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
рвали вони лободу́ на кущах, ялівце́ве ж коріння було їхнім хлібом.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Вони були ви́гнані з-поміж людей, кричали на них, немов на злоді́їв,
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
так що вони пробува́ли в яру́гах долин, по я́мах під земних та скелях,
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
ревіли вони між кущами, збирались під те́рням, —
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
сини нерозумного й діти неславного, вони були ви́гнані з кра́ю!
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
А тепер я став піснею їм, і зробився для них погово́ром.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Вони обриди́ли мене, віддали́лись від мене, і від мойого обличчя не стримали сли́ни,
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
бо Він розв'яза́в мого пояса й мучить мене, то й вони ось вузде́чку із себе відкинули перед обличчям моїм.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
По прави́ці встають жовтодзю́бі, но́ги мені підставляють, і то́пчуть на мене дороги нещастя свого.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
Пори́ли вони мою сте́жку, хо́чуть мати ко́ристь із мойого життя, немає кому їх затримати, —
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
немов через ви́лім широкий прихо́дять, валяються попід румо́вищем.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Оберну́лось страхіття на мене, моя слава проне́слась, як вітер, і, як хмара, мину́лося щастя моє.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
А тепер розливається в мене душа моя, хапають мене дні нещастя!
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
Вночі мої кості від мене віддо́вбуються, а жи́ли мої не вспоко́юються.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
З великої Божої сили зміни́лося тіло моє, і неду́га мене опері́зує, мов той хіто́н.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Він укинув мене до болота, і став я подібний до по́роху й по́пелу.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Я кли́чу до Тебе, та Ти мені відповіді не даєш, я перед Тобою стою́, Ти ж на мене лише придивля́єшся.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Ти зміни́вся мені на жорстокого, мене Ти женеш силою Своєї руки.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
На вітер підняв Ти мене, на нього мене посадив, і робиш, щоб я розтопи́всь на спусто́шення!
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Знаю я: Ти до смерти прова́диш мене, і до дому зібра́ння, яко́го призна́чив для всього живого.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Хіба не простяга́є руки́ потопе́льник, чи він у нещасті своїм не кричить?
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Чи ж не плакав я за бідаре́м? Чи за вбогим душа моя не сумувала?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
Бо чекав я добра́, але лихо прийшло, сподівався я світла, та темно́та прийшла.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Киплять мої ну́трощі й не замовка́ють, зустріли мене дні нещастя,
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
ходжу́ почорнілий без сонця, на зборі встаю та кричу́.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Я став братом шака́лам, а струся́там — това́ришем,
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
моя шкіра зчорніла та й лу́питься з мене, від спеко́ти спали́лися кості мої.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
І стала жало́бою а́рфа моя, а сопі́лка моя — зойком плачли́вим.

< Yobu 30 >