< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
Pero ahora, se burlan de mí los que son más jóvenes que yo, a cuyos antepasados yo rehusé dejar con los perros de mi rebaño,
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
pues ¿para qué me servía la fuerza de sus manos, si su edad madura y su vigor perecieron?
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Están anémicos a causa de la miseria y el hambre. Roen la tierra reseca y huyen a la desolación, al lugar tenebroso y despoblado.
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Arrancan malvas entre los matorrales y se alimentan con raíces de enebro.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Están expulsados de la comunidad. Contra ellos gritan como a ladrones.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
Viven en barrancos espantosos, en cuevas de la tierra y en las peñas.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Aúllan entre los matorrales y se apiñan bajo las ortigas.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Generación de necios, generación sin nombre, echados a latigazos de esta tierra.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
¡Y ahora soy su motivo de mofa y les sirvo de refrán!
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Me repugnan y se alejan de mí. De mi presencia no refrenan su saliva.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Porque Él aflojó la cuerda de mi arco y me afligió, ellos se quitaron el freno frente a mí.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
A mi derecha se levanta el populacho, enredan mis pies, me preparan caminos destructivos,
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
desbaratan mi senda, se aprovechan de mi calamidad y nadie los restringe.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Vienen como abridores de amplia brecha [en el muro] y en medio de la ruinosa tormenta se abalanzan contra mi calamidad.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Los terrores me asaltan de repente, combatieron mi honor como el viento y mi prosperidad desapareció como nube.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
Ahora mi alma se me derrama. Los días de aflicción se apoderaron de mí.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
La noche me taladra los huesos y los dolores que me corroen no descansan.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Una fuerza poderosa desfiguró mi ropa y me aprieta como el cuello de mi abrigo.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Me derribó en el lodo. Quedé como el polvo y la ceniza.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Clamo a Ti, y no me respondes. Me presento, y Tú no me atiendes.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Te volviste cruel conmigo y me persigues con la fuerza de tu mano.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Me levantas, me haces cabalgar sobre el viento y me deshaces en la tormenta.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Porque yo sé que me conduces a la muerte, a la casa de reunión para todos los vivientes.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
¿Sin embargo no extiendes tu mano al que está sobre una pila de ruinas o en su desastre, y por tanto pide socorro?
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
¿No lloré por el afligido? ¿No tuvo compasión mi alma del menesteroso?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
Pero cuando esperaba el bien, me vino el mal. Cuando esperaba luz, me vino oscuridad.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Mis órganos internos se agitan y no reposan. Me confrontan días de aflicción.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Ando ennegrecido, y no por el sol. Me levanto en la congregación y pido ayuda.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Soy hermano de chacales y compañero de avestruces.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Mi piel ennegrecida se me cae, y mis huesos arden de calor.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Por tanto, mi arpa se convirtió en lamento, y mi flauta es la voz de los que lloran.

< Yobu 30 >