< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
А сада смеју ми се млађи од мене, којима отаца не бих хтео метнути са псима стада свог.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
А на шта би ми и била сила руку њихових? У њима беше пропала старост.
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Од сиромаштва и глади самоћаваху бежећи од сува, мрачна, пуста и опустошена места;
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Који браху лободу по честама, и смреково корење беше им храна.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Између људи беху изгоњени и викаше се за њима као за лупежом.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
Живљаху по страшним увалама, по јамама у земљи и у камену.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
По грмовима рикаху, под трњем се скупљаху.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Беху људи никакви и без имена, мање вредни него земља.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
И њима сам сада песма, и постах им прича.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Гаде се на ме, иду далеко од мене и не устежу се пљувати ми у лице.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Јер је Бог одапео моју тетиву и муке ми задао те збацише узду преда мном.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
С десне стране устајаху момци, поткидаху ми ноге, и насипају пут к мени да ме упропасте.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
Раскопаше моју стазу, умножише ми муке, не треба нико да им помаже.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Као широким проломом навиру, и наваљују преко развалина.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Страхоте навалише на ме, и као ветар терају душу моју, и као облак прође срећа моја.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
И сада се душа моја разлива у мени, стигоше ме дани мучни.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
Ноћу пробада ми кости у мени, и жиле моје не одмарају се.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Од тешке силе променило се одело моје, и као огрлица у кошуље моје стеже ме.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Бацио ме је у блато, те сам као прах и пепео.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Вичем к Теби, а Ти ме не слушаш; стојим пред Тобом, а Ти не гледаш на ме.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Претворио си ми се у љута непријатеља; силом руке своје супротиш ми се.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Подижеш ме у ветар, посађујеш ме на њ, и растапаш у мени све добро.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Јер знам да ћеш ме одвести на смрт и у дом одређени свима живима.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Али неће пружити руке своје у гроб; кад их стане потирати, они неће викати.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Нисам ли плакао ради оног који беше у злу? Није ли душа моја жалосна бивала ради убогог?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
Кад се добру надах, дође ми зло; и кад се надах светлости, дође мрак.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Утроба је моја узаврела, и не може да се умири, задесише ме дани мучни.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Ходим црн, не од сунца, устајем и вичем у збору.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Брат постах змајевима и друг совама.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Поцрнела је кожа на мени и кости моје посахнуше од жеге.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Гусле се моје претворише у запевку, и свирала моја у плач.

< Yobu 30 >