< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
Men nu ler de av mig, de som er yngre av år enn jeg, hvis fedre jeg aktet så ringe at jeg ikke vilde sette dem blandt mine fehunder.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Hvad hjelp kunde jeg også ha av dem, de som har mistet all manndomskraft?
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
De er uttæret av nød og sult; de gnager på den tørre mo, som allerede igår var ørk og øde;
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
de plukker melde innunder buskene, og gyvelbuskens røtter er deres brød.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Fra menneskenes samfund jages de ut; folk roper efter dem som efter tyver.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
I fryktelige kløfter må de bo, i huler i jord og berg.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Mellem buskene skriker de, i neslekratt samler de sig,
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
barn av dårer og æreløse folk, pisket ut av landet.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
Og nu er jeg blitt til en spottesang og et ordsprog for dem.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
De avskyr mig, holder sig langt borte fra mig, og mitt ansikt sparer de ikke for spytt;
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
for de har løst sine tøiler og ydmyket mig, og bislet har de kastet av for mine øine.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
Ved min høire side reiser deres yngel sig; mine føtter støter de bort og legger sine ulykkesveier mot mig.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
De bryter op min sti, de gjør hvad de kan for å ødelegge mig, de som selv ingen hjelper har.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Som gjennem en vid revne kommer de; gjennem nedstyrtende murer velter de sig frem.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Redsler har vendt sig mot mig, som stormen forfølger de min ære, og som en sky er min velferd faret bort.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
Og nu utøser min sjel sig i mig; trengsels dager holder mig fast.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
Natten gjennemborer mine ben, så de faller av, og min verk og pine hviler ikke.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Ved Guds store kraft er det blitt slik med mig at min klædning ikke er til å kjenne igjen; den henger tett omkring mig som kraven på min underkjortel.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Han har kastet mig ut i skarnet, så jeg er blitt lik støv og aske.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Jeg skriker til dig, men du svarer mig ikke; jeg står der, og du bare ser på mig.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Du er blitt grusom mot mig, med din sterke hånd forfølger du mig.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Du løfter mig op i stormen, du lar mig fare avsted, og du lar mig forgå i dens brak;
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
for jeg vet at du fører mig til døden, til den bolig hvor alt levende samles.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Dog, rekker ikke mennesket ut sin hånd når alt synker i grus? Skriker han ikke om hjelp når han er kommet i ulykke?
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Gråt jeg ikke selv over den som hadde hårde dager? Sørget ikke min sjel over den fattige?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
For jeg ventet godt, men det kom ondt; jeg håpet på lys, men det kom mørke.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Mine innvoller koker og er ikke stille; trengsels dager er kommet over mig.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Sort går jeg omkring, men ikke av solens hete; midt iblandt folk reiser jeg mig og roper om hjelp.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Jeg er blitt en bror av sjakaler og en stallbror av strutser.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Min hud er sort og faller av mig, og mine ben er brent av hete.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Og min citar er blitt til sorg, og min fløite til gråt og klage.

< Yobu 30 >