< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
Et maintenant, ceux qui sont plus jeunes que moi se moquent de moi, ceux dont j’aurais dédaigné de mettre les pères avec les chiens de mon troupeau.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Même à quoi m’aurait servi la force de leurs mains? La vigueur a péri pour eux.
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Desséchés par la disette et la faim, ils s’enfuient dans les lieux arides, dès longtemps désolés et déserts;
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Ils cueillent le pourpier de mer parmi les broussailles, et, pour leur pain, la racine des genêts.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Ils sont chassés du milieu [des hommes], (on crie après eux comme après un voleur, )
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
Pour demeurer dans des gorges affreuses, dans les trous de la terre et des rochers;
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Ils hurlent parmi les broussailles, ils se rassemblent sous les ronces:
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Fils d’insensés, et fils de gens sans nom, ils sont chassés du pays.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
Et maintenant, je suis leur chanson et je suis le sujet de leur entretien.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Ils m’ont en horreur, ils se tiennent loin de moi, et n’épargnent pas à ma face les crachats;
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Car Il a délié ma corde et m’a affligé: ils ont jeté loin [tout] frein devant moi.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
Cette jeune engeance se lève à ma droite; ils poussent mes pieds et préparent contre moi leur chemin pernicieux;
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
Ils détruisent mon sentier, ils contribuent à ma calamité, sans que personne leur vienne en aide;
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Ils viennent comme par une large brèche, ils se précipitent au milieu du fracas.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Des terreurs m’assaillent, elles poursuivent ma gloire comme le vent, et mon état de sûreté est passé comme une nuée.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
Et maintenant, mon âme se répand en moi: les jours d’affliction m’ont saisi.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
La nuit perce mes os [et les détache] de dessus moi, et ceux qui me rongent ne dorment pas;
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Par leur grande force ils deviennent mon vêtement; ils me serrent comme le collet de ma tunique.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Il m’a jeté dans la boue, et je suis devenu comme la poussière et la cendre.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Je crie à toi, et tu ne me réponds pas; je me tiens là, et tu me regardes!
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Tu t’es changé pour moi en [ennemi] cruel; tu me poursuis avec la force de ta main.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Tu m’enlèves sur le vent, tu fais qu’il m’emporte, et tu dissous ma substance.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Car je sais que tu m’amènes à la mort, la maison de rassemblement de tous les vivants.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Toutefois, dans sa ruine, n’étend-il pas la main, et, dans sa calamité, ne jette-t-il pas un cri [de détresse]?
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
N’ai-je pas pleuré sur celui pour qui les temps étaient durs, et mon âme n’a-t-elle pas été attristée pour le pauvre?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
Car j’attendais le bien, et le mal est arrivé; je comptais sur la lumière, et l’obscurité est venue.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Mes entrailles bouillonnent et ne cessent pas; les jours d’affliction sont venus sur moi.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Je marche tout noirci, mais non par le soleil; je me lève dans l’assemblée, je crie;
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Je suis devenu le frère des chacals et le compagnon des autruches.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Ma peau devient noire [et se détache] de dessus moi, et mes os sont brûlés par la sécheresse;
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Et ma harpe est changée en deuil, et mon chalumeau est devenu la voix des pleureurs.

< Yobu 30 >