< Yobu 30 >
1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
« Mais maintenant, ceux qui sont plus jeunes que moi me tournent en dérision, dont j'ai considéré les pères comme indignes d'être mis avec mes chiens de berger.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
A quoi me sert la force de leurs mains? des hommes chez qui l'âge mûr a péri?
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Ils sont décharnés par le manque et la famine. Ils rongent la terre aride, dans la pénombre du désert et de la désolation.
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Ils cueillent des herbes salées près des buissons. Les racines de l'arbre à balais sont leur nourriture.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Ils sont chassés du milieu des hommes. Ils crient après eux comme après un voleur,
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
de sorte qu'ils vivent dans des vallées effrayantes, et dans les trous de la terre et des rochers.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Ils braillent dans les buissons. Ils sont rassemblés sous les orties.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Ce sont des enfants de fous, oui, des enfants de méchants. Ils ont été chassés du pays à coups de fouet.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
« Maintenant, je suis devenu leur chant. Oui, je suis un mot d'ordre pour eux.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Ils m'abhorrent, ils se tiennent à l'écart de moi, et n'hésitez pas à me cracher au visage.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Car il a détaché son cordon, et m'a fait souffrir; et ils se sont libérés de toute contrainte devant moi.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
A ma droite se lève la populace. Ils ont repoussé mes pieds. Ils ont jeté contre moi leurs méthodes de destruction.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
Ils marquent mon chemin. Ils favorisent ma destruction sans l'aide de personne.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Ils arrivent comme par une large brèche. Ils s'enroulent au milieu des ruines.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Les terreurs se sont retournées contre moi. Ils chassent mon honneur comme le vent. Mon bien-être s'est éteint comme un nuage.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
« Maintenant mon âme est répandue au-dedans de moi. Des jours d'affliction se sont emparés de moi.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
Au temps de la nuit, mes os sont percés en moi, et les douleurs qui me rongent ne prennent aucun repos.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Mon vêtement est défiguré par une grande force. Il me lie comme le col de ma tunique.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Il m'a jeté dans la boue. Je suis devenu comme de la poussière et des cendres.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Je crie vers toi, et tu ne me réponds pas. Je me lève, et tu me regardes.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Tu t'es retourné pour être cruel envers moi. De la force de ta main, tu me persécutes.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Tu me soulèves au vent, et tu me pousses avec lui. Vous me dissolvez dans la tempête.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Car je sais que tu me feras mourir, à la maison désignée pour tous les vivants.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
« Cependant, on ne tend pas la main dans sa chute? Ou dans sa calamité donc crier au secours?
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
N'ai-je pas pleuré sur celui qui était dans la détresse? Mon âme n'a-t-elle pas été affligée par les nécessiteux?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
J'ai cherché le bien, et le mal est venu. Quand j'ai attendu la lumière, l'obscurité est venue.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Mon cœur est troublé, et ne se repose pas. Des jours d'affliction sont venus sur moi.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Je suis en deuil sans le soleil. Je me lève dans l'assemblée, et je crie à l'aide.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Je suis un frère pour les chacals, et un compagnon des autruches.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Ma peau devient noire et se détache de moi. Mes os sont brûlés par la chaleur.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
C'est pourquoi ma harpe s'est changée en deuil, et ma pipe dans la voix de ceux qui pleurent.