< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
But now they that are younger than I hold me in derision, Whose fathers I would have disdained to set with the dogs of my flock.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Of what use to me would be even the strength of their hands, To whom old age is lost?
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
By want and hunger they are famished; They gnaw the dry desert, The darkness of desolate wastes.
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
They gather purslain among the bushes, And the root of the broom is their bread.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
They are driven from the society of men; There is a cry after them as after a thief.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
They dwell in gloomy valleys, In caves of the earth and in rocks.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
They bray among the bushes; Under the brambles are they stretched out.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
An impious and low-born race, They are beaten out of the land.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
And now I am become their song; Yea, I am their by-word!
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
They abhor me, they stand aloof from me; They forbear not to spit before my face.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Yea, they let loose the reins, and humble me; They cast off the bridle before me.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
On my right hand riseth up the brood; They thrust away my feet; They cast up against me their destructive ways.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
They break up my path; They hasten my fall, —They who have no helper!
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
They come upon me as through a wide breach; Through the ruins they rush in upon me.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Terrors are turned against me; They pursue my prosperity like the wind, And my welfare passeth away like a cloud.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
And now my soul poureth itself out upon me; Days of affliction have taken hold of me.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
By night my bones are pierced; they are torn from me, And my gnawers take no rest.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Through the violence of my disease is my garment changed; It bindeth me about like the collar of my tunic.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
He hath cast me into the mire, And I am become like dust and ashes.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
I call upon Thee, but thou dost not hear me; I stand up before thee, but thou regardest me not.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Thou art become cruel to me; With thy strong hand dost thou lie in wait for me.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Thou liftest me up, and causest me to ride upon the wind; Thou meltest me away in the storm.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
I know that thou wilt bring me to death, To the place of assembly for all the living.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
When He stretcheth out his hand, prayer availeth nothing; When He bringeth destruction, vain is the cry for help.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Did not I weep for him that was in trouble? Was not my soul grieved for the poor?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
But when I looked for good, then evil came; When I looked for light, then came darkness.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
My bowels boil, and have no rest; Days of anguish have come upon me.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
I am black, but not by the sun; I stand up, and utter my cries in the congregation.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
I am become a brother to jackals, And a companion to ostriches.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
My skin is black, and falleth from me, And my bones burn with heat.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
My harp also is turned to mourning, And my pipe to notes of grief.

< Yobu 30 >