< Yobu 30 >
1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
“And now, laughed at me, Have the younger in days than I, Whose fathers I have loathed to set With the dogs of my flock.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Also—the power of their hands, why [is it] to me? On them old age has perished.
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
With want and with harsh famine, They are gnawing a dry place [in] the recent night, [In] desolation and ruin,
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Those cropping mallows near a shrub, And their food [is] root of broom trees.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
They are cast out from the midst (They shout against them as a thief),
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
To dwell in a frightful place of valleys, Holes of earth and clefts.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
They groan among shrubs, They are gathered together under nettles.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Sons of folly—even sons without name, They have been struck from the land.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
And now, I have been their song, And I am to them for a byword.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
They have detested me, They have kept far from me, And from before me have not spared to spit.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Because He loosed His cord and afflicts me, And the bridle from before me, They have cast away.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
A brood arises on the right hand, They have cast away my feet, And they raise up against me, Their paths of calamity.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
They have broken down my path, They profit by my calamity: He has no helper.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
They come as a wide breach, Under the desolation have rolled themselves.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
He has turned terrors against me, It pursues my abundance as the wind, And as a thick cloud, My safety has passed away.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
And now, in me my soul pours itself out, Days of affliction seize me.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
[At] night my bone has been pierced in me, And my gnawing [pain] does not lie down.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
By the abundance of power, Is my clothing changed, As the mouth of my coat it girds me.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Casting me into mire, And I have become like dust and ashes.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
I cry to You, And You do not answer me, I have stood, and You consider me.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
You are turned to be fierce to me, With the strength of Your hand, You oppress me.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
You lift me up, You cause me to ride on the wind, And You melt—You level me.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
For I have known You bring me back [to] death, And [to] the house appointed for all living.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Surely not against the heap Does He send forth the hand, Though they have safety in its ruin.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Did I not weep for him whose day is hard? My soul has grieved for the needy.
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
When I expected good, then comes evil, And I wait for light, and darkness comes.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
My bowels have boiled, and have not ceased, Days of affliction have gone before me.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
I have gone mourning without the sun, I have risen, I cry in an assembly.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
I have been a brother to dragons, And a companion to daughters of the ostrich.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
My skin has been black on me, And my bone has burned from heat,
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
And my harp becomes mourning, And my pipe the sound of weeping.”