< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
BUT now they that are younger than I have me in derision, whose fathers I would have disdained to have set with the dogs of my flock.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Yea, whereto might the strength of their hands profit me, in whom old age was perished?
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
For want and famine they were solitary; fleeing into the wilderness in former time desolate and waste.
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Who cut up mallows by the bushes, and juniper roots for their meat.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
They were driven forth from among men, (they cried after them as after a thief; )
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
To dwell in the clifts of the valleys, in caves of the earth, and in the rocks.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Among the bushes they brayed; under the nettles they were gathered together.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
They were children of fools, yea, children of base men: they were viler than the earth.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
And now am I their song, yea, I am their byword.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
They abhor me, they flee far from me, and spare not to spit in my face.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Because he hath loosed my cord, and afflicted me, they have also let loose the bridle before me.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
Upon my right hand rise the youth; they push away my feet, and they raise up against me the ways of their destruction.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
They mar my path, they set forward my calamity, they have no helper.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
They came upon me as a wide breaking in of waters: in the desolation they rolled themselves upon me.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Terrors are turned upon me: they pursue my soul as the wind: and my welfare passeth away as a cloud.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
And now my soul is poured out upon me; the days of affliction have taken hold upon me.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
My bones are pierced in me in the night season: and my sinews take no rest.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
By the great force of my disease is my garment changed: it bindeth me about as the collar of my coat.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
He hath cast me into the mire, and I am become like dust and ashes.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
I cry unto thee, and thou dost not hear me: I stand up, and thou regardest me not.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Thou art become cruel to me: with thy strong hand thou opposest thyself against me.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Thou liftest me up to the wind; thou causest me to ride upon it, and dissolvest my substance.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
For I know that thou wilt bring me to death, and to the house appointed for all living.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Howbeit he will not stretch out his hand to the grave, though they cry in his destruction.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Did not I weep for him that was in trouble? was not my soul grieved for the poor?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
When I looked for good, then evil came unto me: and when I waited for light, there came darkness.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
My bowels boiled, and rested not: the days of affliction prevented me.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
I went mourning without the sun: I stood up, and I cried in the congregation.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
I am a brother to dragons, and a companion to owls.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
My skin is black upon me, and my bones are burned with heat.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
My harp also is turned to mourning, and my organ into the voice of them that weep.

< Yobu 30 >