< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
But now the younger in time scorn me, whose fathers I would not have set with the dogs of my flock:
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
The strength of whose hands was to me as nothing, and they were thought unworthy of life itself.
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Barren with want and hunger, who gnawed in the wilderness, disfigured with calamity and misery.
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
And they ate grass, and barks of trees, and the root of junipers was their food.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Who snatched up these things out of the valleys, and when they had found any of them, they ran to them with a cry.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
They dwelt in the desert places of torrents, and in caves of earth, or upon the gravel.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
They pleased themselves among these kind of things, and counted it delightful to be under the briers.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
The children of foolish and base men, and not appearing at all upon the earth.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
Now I am turned into their song, and am become their byword.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
They abhor me, and flee far from me, and are not afraid to spit in my face.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
For he hath opened his quiver, and hath afflicted me, and hath put a bridle into my mouth.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
At the right hand of my rising, my calamities forthwith arose: they have overthrown my feet, and have overwhelmed me with their paths as with waves.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
They have destroyed my ways, they have lain in wait against me, and they have prevailed, and there was none to help.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
They have rushed in upon me, as when a wall is broken, and a gate opened, and have rolled themselves down to my miseries.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
I am brought to nothing: as a wind thou hast taken away my desire: and my prosperity hath passed away like a cloud.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
And now my soul fadeth within myself, and the days of affliction possess me.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
In the night my bone is pierced with sorrows: and they that feed upon me, do not sleep.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
With the multitude of them my garment is consumed, and they have girded me about, as with the collar of my coat.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
I am compared to dirt, and am likened to embers and ashes.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
I cry to thee, and thou hearest me not: I stand up, and thou dost not regard me.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Thou art changed to be cruel toward me, and in the hardness of thy hand thou art against me.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Thou hast lifted me up, and set me as it were upon the wind, and thou hast mightily dashed me.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
I know that thou wilt deliver me to death, where a house is appointed for every one that liveth.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
But yet thou stretchest not forth thy hand to their consumption: and if they shall fall down thou wilt save.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
I wept heretofore for him that was afflicted, and my soul had compassion on the poor.
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
I expected good things, and evils are come upon me: I waited for light, and darkness broke out.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
My inner parts have boiled without any rest, the days of affliction have prevented me.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
I went mourning without indignation; I rose up, and cried in the crowd.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
I was the brother of dragons, and companion of ostriches.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
My skin is become black upon me, and my bones are dried up with heat.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
My harp is turned to mourning, and my organ into the voice of those that weep.

< Yobu 30 >