< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
Но сега ми се подсмиват по-младите от мене, Чиито бащи не бих приел да туря с кучетата на стадото си;
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Защото в що можеше да ме ползува силата на ръцете им, Човеци, чиято жизненост бе изчезнала?
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
От немотия и глад те бяха измършавели; Гризяха изсушената земя, отдавна пуста и опустошена;
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Между храстите късаха слез, И корените на смрика им бяха за храна.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Бяха изпъдени измежду човеците, Които викаха подир тебе като подир крадци.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
Живееха в пукнатините на долините, В дупките на земята и на скалите.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Ревяха между храстите. Събираха се между тръните;
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Безумни и безчестни, Те бидоха изгонени от земята.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
А сега аз им станах песен, Още им съм и поговорка.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Гнусят се от мене, отдалечават се от мене, И не се свенят да плюят в лицето ми.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Тъй като Бог е съсипал достолепието ми и ме е смирил. То и те се разюздаха пред мене.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
Отдясно въстават тия изроди, Тласкат нозете ми, И приготовляват против мене гибелните си намерения,
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
Развалят пътя ми, Увеличават нещастието ми, И то без да имат помощници.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Идат като през широк пролом; Под краха нахвърлят се върху мене.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Ужаси се обърнаха върху мене; Като вятър гонят достолепието ми; И благополучието ми премина като облак.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
И сега душата ми се излива в мене; Скръбни дни ме постигнаха.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
През нощта костите ми се пронизват в мене, И жилите ми не си почиват.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Само с голямо усилие се променява дрехата ми; Тя ме стига както яката на хитона ми.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Бог ме е хвърлил в калта; И аз съм заприличал на пръст и на прах.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Викам към Тебе, но не ми отговаряш; Стоя, и Ти просто ме поглеждаш.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Обърнал си се да се показваш жесток към мене; С мощната Си ръка ми враждуваш;
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Издигаш ме, възкачваш ме на вятъра, И стопяваш ме в бурята.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Зная наистина, че ще ме докараш до смърт, И до дома, който е определен за всичките живи.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Обаче в падането си човек няма ли да простре ръка, Или да нададе вик в бедствието си?
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Не плаках ли аз за онзи, който бе отруден? И не се ли оскърби душата ми за сиромаха?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
Когато очаквах доброто, тогава дойде злото; И когато ожидах виделината, тогава дойде тъмнината.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Червата ми възвират, и не си почиват; Скръбни дни ме постигнаха.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Ходя почернял, но не от слънцето; Ставам в събранието и викам за помощ.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Станах брат на чакалите, И другар на камилоптиците.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Кожата ми почерня на мене, И костите ми изгоряха от огън.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Затова арфата ми се измени в ридание, И свирката ми в глас на плачещи.

< Yobu 30 >