< Yobu 3 >

1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
Baada ya hayo, Ayubu akafunua kinywa chake na kuilani siku aliyozaliwa.
2 Ndipo Yobu anati:
Akasema,
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
“Na ipotelee mbali siku niliyozaliwa mimi, usiku uliosema, 'Mimba ya mtoto wa kiume imetungwa.'
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Siku hiyo na iwe giza; Mungu toka juu asiifikilie, wala mwanga usiiangazie.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Ishikwe na giza na giza la mauti liwe lake. Wingu na likae juu yake; kila kitu kiifanyacho siku kuwa giza kweli na kiitishe.
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
Usiku huo, na ukamatwe na giza tororo. Usihesabiwe miongoni mwa siku za mwaka; na usiwekwe katika hesabu ya miezi.
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Tazama, usiku huo na uwe tasa; na sauti ya shangwe isiwe ndani yake.
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Na wailani siku hiyo, hao wafahamuo namna ya kumuamsha lewiathani.
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
Nyota za mapambazuko yake zitiwe giza. Siku hiyo iutafute mwanga, lakini isiupate; wala makope ya mapambazuko isiyaone,
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
kwasababu haikuifunga milango ya tumbo la mama yangu, na kwasababu haikunifichia taabu machoni pangu.
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
Kwanini si-kufa wakati lipotokeza katika tumbo la uzazi? Kwanini sikuitoa roho yangu hapo mama aliponizaa?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
kwanini magoti yake yalinipokea? Kwanini maziwa yake yanipokee hata ninyonye?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
Kwa sasa ningelikuwa nimelala chini kimya kimya. Ningelala usingizi na kupata pumziko
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
pamoja na wafalme na washauri wa dunia, ambao walijijengea makaburi ambayo sasa ni magofu.
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
Au Ningelikuwa nimelala pamoja na wakuu wenye dhahabu, waliozijaza nyumba zao fedha.
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
Au pengine ningekuwa sijazaliwa, kama watoto wachanga wasio uona mwanga kabisa.
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
Huko waovu huacha kusumbua; huko waliochoka hupumzika.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
Huko wafungwa kwa pamoja hupata amani; hawaisikii sauti ya msimamizi wa watumwa.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
Wote wadogo na watu maarufu wako huko; mtumishi yuko huru kwa bwana wake huko.
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
Kwa nini yeye aliye mashakani kupewa mwanga? Kwa nini hao wenye uchungu moyoni kupewa uhai,
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
ambao hutamani mauti lakini hawapati; ambao huyachimbulia mauti zaidi ya kutafuta hazina iliyofichika?
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
Kwa nini kupewa mwanga ambao hushangilia mno na kufurahi walionapo kaburi?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
Kwanini kupewa mwanga mtu ambaye njia zake zimefichika, mtu ambaye Mungu amemzungushia uwa?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
Kwa kuwa kushusha kwangu pumzi kwatokea badala ya kula; kuugua kwangu kumemiminika kama maji.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
Maana jambo lile niliogopalo limenipata; nalo linitialo hofu limenijilia.
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
Mimi sioni raha, sipati utulivu, na sipati pumziko; badala yake huja taabu.”

< Yobu 3 >