< Yobu 3 >

1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
Depois disto Jó abriu sua boca, e amaldiçoou seu dia.
2 Ndipo Yobu anati:
Pois Jó respondeu, e disse:
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Pereça o dia em que nasci, e a noite [em que] se disse: Um homem foi concebido.
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Torne-se aquele dia em trevas; Deus não lhe dê atenção desde acima, nem claridade brilhe sobre ele.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Reivindiquem-no para si trevas e sombra de morte; nuvens habitem sobre ele; a escuridão do dia o espante.
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
Tome a escuridão aquela noite; não seja contada entre os dias do ano, nem faça parte do número dos meses.
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Ah se aquela noite fosse solitária, e música de alegria não viesse a ela!
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Amaldiçoem-na os que amaldiçoam o dia, os que se preparam para levantar seu pranto.
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
Escureçam-se as estrelas de sua manhã; espere a luz, e não venha, e as pálpebras não vejam o amanhecer;
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
Pois não fechou as portas do ventre onde eu estava, nem escondeu de meus olhos o sofrimento.
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
Por que eu não morri desde a madre, ou perdi a vida ao sair do ventre?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
Por que joelhos me receberam? E por que seios me amamentaram?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
Pois agora eu jazeria e repousaria; dormiria, e então haveria repouso para mim;
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
Com os reis e os conselheiros da terra, que edificavam para si os desertos;
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
Ou com os príncipes que tinham ouro, que enchiam suas casas de prata.
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
Ou [por que] não fui como um aborto oculto, como as crianças que nunca viram a luz?
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
Ali os maus deixam de perturbar, e ali repousam os cansados de forças.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
Ali os prisioneiros juntamente repousam; [e] não ouvem a voz do opressor.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
Ali estão o pequeno e o grande; e o servo livre [está] de seu senhor.
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
Por que se dá luz ao sofredor, e vida aos amargos de alma,
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
Que esperam a morte, e ela não chega, e que a buscam mais que tesouros;
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
Que saltam de alegram e ficam contentes quando acham a sepultura?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
[E também] ao homem cujo caminho é oculto, e a quem Deus [o] encobriu?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
Pois antes do meu pão vem meu suspiro; e meus gemidos correm como águas.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
Pois aquilo eu temia tanto veio a mim, e aquilo que tinha medo me aconteceu.
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
Não tenho tido descanso, nem tranquilidade, nem repouso; mas perturbação veio sobre mim.

< Yobu 3 >