< Yobu 3 >

1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
MAHOPE iho o keia, pane ae la ko Ioba waha, a hoino aku la ia i kona la.
2 Ndipo Yobu anati:
Olelo mai la o Ioba, i mai la,
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
E poho wale iho ka la a'u i hanau ai, A me ka po i oleloia, ua hapaiia he keikikane.
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
E lilo ua la la i pouli; Mai manao ke Akua ia mai luna mai, Aole hoi e alohi mai ka malamalama maluna ona.
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
E haukae ka pouli a me ka malu make ia la; E kau ka naulu maluna ona; E hooweliweli na wela o ka la ia ia.
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
A o ua po la, e lawe aku ka pouli ia ia; Aole e hui pu ia oia me na la o ka makahiki; Mai hookomoia oia iloko o ka helu ana o na malama.
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Aia hoi, o ua po la, e hooneoneoia oia; Aole e hookomoia ka leo olioli iloko ona.
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Na lakou ia e hoino, na ka poe e hoino ana i ua la la, Ka poe makaukau no ke kanikau ana.
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
E hoopouliia na hoku o kona wa molehulehu: E kali aku ia i ka malamalama, a loaa ole; Aole hoi ia e ike i ka wehe ana o ke alaula.
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
No ka mea, aole ia i hoopaa i na puka o ka opu o kuu makuwahine, Aole hoi ia i huna i ka popilikia mai ko'u maka aku.
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
No ke aha la i make ole ai au mai ka opu mai? No ke aha la i kaili ole ia kuu ea i kuu puka ana mai ka opu mai?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
No ke aha la i kokua ai na kuli ia'u? No ke aha hoi na u, i omo aku ai au?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
Alaila, ua moe iho au ano, a ua maluhia iho, Ua hiamoe iho la au, alaila ua maha iho la au,
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
Me na'lii, a me na kuhina o ka honua, Ka poe i kukulu i na wahi neoneo no lakou:
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
Me na keiki alii paha, ka poe mea gula, Me ka poe i hoopiha i ko lakou mau hale i ke kala:
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
A, me he mea la i hanau i ka wa, ua ole au; Me na keiki ike ole i ka malamalama.
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
Malaila e hooki ai ka poe hewa i ka hana kolohe ana; Malaila hoi e hoomahaia'i ka poe i luhi o ka ikaika.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
A e hoomaha pu ia'i hoi ka poe pio; Aole lakou i lohe i ka leo o ka mea hooluhi.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
O ka mea uuku, a me ka mea nui, aia no malaila; A o ke kauwa, ua kaawale ia mai kona haku aku.
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
No ke aha la i haawiia mai ai ka malamalama i ka mea popilikia, A me ke ola i ka mea eha ma ka naau?
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
Ka poe e kali ana i ka make, aole i hiki mai, A ua oi ko lakou eli ana ia mea, mamua o na waiwai i hunaia;
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
I ka poe hauoli nui me ka olioli, I ka wa i loaa'i ia lakou ka luakupapau?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
I ke kanaka i hunaia kona aoao, I ka mea a ke Akua i hoopuni ai?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
No ka mea, ua hiki pu mai ko'u kaniuhu ana me kuu ai ana, A ua nininiia'ku ko'u uwe ana e like me na wai.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
No ka mea, ua makau au i ka mea makau, a ua hiki mai ia maluna o'u, A o ka mea a'u i weliweli ai ua hele mai ia io'u nei.
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
Aole au i pomaikai, aole hoi i oluolu, Aole hoi i maha; aka, hiki mai ka popilikia.

< Yobu 3 >