< Yobu 3 >

1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
after so to open Job [obj] lip his and to lighten [obj] day his
2 Ndipo Yobu anati:
and to answer Job and to say
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
to perish day to beget in/on/with him and [the] night to say to conceive great man
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
[the] day [the] he/she/it to be darkness not to seek him god from above and not to shine upon him light
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
to redeem: redeem him darkness and shadow to dwell upon him cloud to terrify him darkness day
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
[the] night [the] he/she/it to take: take him darkness not to rejoice in/on/with day year in/on/with number month not to come (in): come
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
behold [the] night [the] he/she/it to be solitary not to come (in): come triumphing in/on/with him
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
to curse him to curse day [the] ready to rouse Leviathan
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
to darken star twilight his to await to/for light and nothing and not to see: see in/on/with eyelid dawn
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
for not to shut door belly: womb my and to hide trouble from eye my
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
to/for what? not from womb to die from belly: womb to come out: produce and to die
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
why? to meet me knee and what? breast for to suckle
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
for now to lie down: lay down and to quiet to sleep then to rest to/for me
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
with king and to advise land: country/planet [the] to build desolation to/for them
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
or with ruler gold to/for them [the] to fill house: home their silver: money
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
or like/as miscarriage to hide not to be like/as infant not to see: see light
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
there wicked to cease turmoil and there to rest weary strength
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
unitedness prisoner to rest not to hear: hear voice to oppress
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
small and great: large there he/she/it and servant/slave free from lord his
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
to/for what? to give: give to/for labour(er) light and life to/for bitter soul
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
[the] to wait to/for death and nothing he and to search him from treasure
22 amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
[the] glad to(wards) rejoicing to rejoice for to find grave
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
to/for great man which way: journey his to hide and to fence god about/through/for him
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
for to/for face: before food: bread my sighing my to come (in): come and to pour like/as water roaring my
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
for dread to dread and to come me and which to fear to come (in): come to/for me
26 Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”
not to prosper and not to quiet and not to rest and to come (in): come turmoil

< Yobu 3 >