< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Och Job hof åter upp sitt ordspråk, och sade:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Ack! att jag vore såsom uti de förra månader, uti de dagar då Gud bevarade mig.
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Då hans lykta sken öfver mitt hufvud, och jag i mörkrena gick vid hans ljus;
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Såsom jag var i min ungdoms tid, då Guds hemlighet var öfver mina hyddo;
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
Då den Allsmägtige ännu med mig var, och mine tjenare allt omkring mig;
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
Då jag tvådde min väg uti smör, och hälleberget utgöt mig oljoflodar;
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Då jag utgick till stadsporten, och lät bereda mig mitt säte på gatone;
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Då mig ynglingar sågo, och undstungo sig, och de gamle uppstodo för mig;
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Då de öfverste igen vände att tala, och lade sina hand på sin mun;
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
Då Förstarnas röst gömde sig undan, och deras tunga lådde vid deras gom.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
Ty hvilkens öra mig hörde, den prisade mig saligan; och hvilkens öga mig såg, den vittnade om mig.
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Förty jag halp den fattiga, som ropade, och den faderlösa, som ingen hjelpare hade.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
Dens välsignelse, som förgås skulle, kom öfver mig; och jag tröstade enkones hjerta.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Rättfärdighet var min klädebonad, den iklädde jag såsom en kjortel; och min dom var min skrud.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Jag var dens blindas öga, och dens haltas fot.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Jag var de fattigas fader, och hvilken sak jag icke visste, den utfrågade jag.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
Jag sönderslog dens orättfärdigas oxlatänder, och tog rofvet utu hans tänder.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
Jag tänkte: Jag vill dö uti mitt näste, och göra mina dagar många såsom sand.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
Min säd gick upp af vätsko, och dagg blef öfver min årsväxt.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
Min härlighet förnyade sig för mig, och min båge förvandlade sig i mine hand.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
De hörde mig, och tigde; och vaktade uppå mitt råd.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Efter min ord talade ingen mer, och mitt tal dröp på dem.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
De vaktade på mig såsom på regn, och uppgapade med munnen såsom efter aftonregn.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Om jag log till dem, förläto de sig intet deruppå; och torde intet bedröfva mig.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
När jag ville komma till deras handlingar, så måste jag sitta främst; och bodde såsom en Konung ibland krigsfolk, då jag hugsvalade dem som sorgfulle voro.

< Yobu 29 >