< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
E Jó continuou a falar seu discurso, dizendo:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Ah quem me dera que fosse como nos meses passados! Como nos dias em que Deus me guardava!
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Quando ele fazia brilhar sua lâmpada sobre minha cabeça, e eu com sua luz caminhava pelas trevas,
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Como era nos dias de minha juventude, quando a amizade de Deus estava sobre minha tenda;
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
Quando o Todo-Poderoso ainda estava comigo, meus filhos ao redor de mim;
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
Quando eu lavava meus passos com manteiga, e da rocha me corriam ribeiros de azeite!
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Quando eu saía para a porta da cidade, [e] na praça preparava minha cadeira,
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Os rapazes me viam, e abriam caminho; e os idosos se levantavam, e ficavam em pé;
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Os príncipes se detinham de falar, e punham a mão sobre a sua boca;
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
A voz dos líderes se calava, e suas línguas se apegavam a céu da boca;
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
O ouvido que me ouvia me considerava bem-aventurado, e o olho que me via dava bom testemunho de mim.
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Porque eu livrava ao pobre que clamava, e ao órfão que não tinha quem o ajudasse.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
A bênção do que estava a ponto de morrer vinha sobre mim; e eu fazia o coração da viúva ter grande alegria.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Vestia-me de justiça, e ela me envolvia; e meu juízo era como um manto e um turbante.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Eu era olhos para o cego, e pés para o manco.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Aos necessitados eu era pai; e a causa que eu não sabia, investigava com empenho.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
E quebrava os queixos do perverso, e de seus dentes tirava a presa.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
E eu dizia: Em meu ninho expirarei, e multiplicarei [meus] dias como areia.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
Minha raiz se estendia junto às águas, e o orvalho ficava de noite em meus ramos.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
Minha honra se renovava em mim, e meu arco se revigorava em minha mão.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Ouviam-me, e esperavam; e se calavam ao meu conselho.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Depois de minha palavra nada replicavam, e minhas razões gotejavam sobre eles.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
Pois esperavam por mim como pela chuva, e abriam sua boca como para a chuva tardia.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Se eu me ria com eles, não acreditavam; e não desfaziam a luz de meu rosto.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Eu escolhia o caminho para eles, e me sentava à cabeceira; e habitava como rei entre as tropas, como o consolador dos que choram.

< Yobu 29 >