< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
E proseguiu Job em proferir o seu dito, e disse:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Ah! quem me dera ser como eu fui nos mezes passados! como nos dias em que Deus me guardava!
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Quando fazia resplandecer a sua candeia sobre a minha cabeça e quando eu pela sua luz caminhava pelas trevas:
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Como era nos dias da minha mocidade, quando o segredo de Deus estava sobre a minha tenda:
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
Quando o Todo-poderoso ainda estava comigo, e os meus meninos em redor de mim.
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
Quando lavava os meus passos na manteiga, e da rocha me corriam ribeiros de azeite:
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Quando sahia a porta pela cidade, e na praça fazia preparar a minha cadeira:
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Os moços me viam, e se escondiam, e até os edosos se levantavam e se punham em pé:
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Os principes continham as suas palavras, e punham a mão sobre a sua bocca:
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
A voz dos chefes se escondia: e a sua lingua se pegava ao seu paladar:
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
Ouvindo-me algum ouvido, me tinha por bemaventurado: vendo-me algum olho, dava testemunho de mim;
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Porque eu livrava o miseravel, que clamava: como tambem o orfão que não tinha quem o soccoresse.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
A benção do que ia perecendo vinha sobre mim, e eu fazia que jubilasse o coração da viuva.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Vestia-me da justiça: e ella me servia de vestido: como manto e diadema era o meu juizo.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Eu fui o olho do cego, como tambem os pés do coxo:
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Aos necessitados era pae, e as causas de que eu não tinha conhecimento inquiria com diligencia;
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
E quebrava os queixaes do perverso, e dos seus dentes tirava a preza.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
E dizia: No meu ninho expirarei, e multiplicarei os meus dias como a areia.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
A minha raiz se estendia junto ás aguas, e o orvalho fazia assento sobre os meus ramos;
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
A minha honra se renovava em mim, e o meu arco se reforçava na minha mão.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Ouvindo-me esperavam, e em silencio attendiam ao meu conselho.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Acabada a minha palavra, não replicavam, e minhas razões distillavam sobre elles;
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
Porque me esperavam, como a chuva; e abriam a sua bocca, como a chuva tardia
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Se me ria para elles, não o criam, e não faziam abater a luz do meu rosto;
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Eu escolhia o seu caminho, assentava-me como chefe, e habitava como rei entre as tropas: como aquelle que consola os que pranteiam.

< Yobu 29 >