< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Då heldt Job fram med talen sin og sagde:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
«Å, var eg som i fordums måna’r, som den gong Gud mi verja var,
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
då yver meg hans lampa skein, som lyste meg i myrkret fram,
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
slik som eg var i mogne manndom, då Gud var ven i huset mitt,
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
då Allvald endå med meg var, og mine born eg kring meg såg,
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
då eg i fløyte foten tvådde, og olje rann av fjellet nær meg,
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
då eg til porten steig i byen, og sessen min på torget tok!
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Ungdomen såg meg, løynde seg; dei gamle reiste seg og stod;
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
hovdingar stogga midt i talen og lagde handi på sin munn;
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
og røysti tagna hjå dei gjæve, og tunga seg til gomen kleimde;
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
dei som meg høyrde, sælka meg, og dei som såg meg, vitna for meg.
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Eg berga arming når han ropa, og farlaus som var utan hjelp;
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
velsigning fekk eg frå forkomne, og enkjor fekk eg til å jubla.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Rettferd var min, eg hennar bunad; rett var mi kappa og mi kruna.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Eg for den blinde auga var, og føter var eg for den halte.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Ein far eg var for fatigfolk; eg for ukjende saki granska.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
På brotsmann tennerne eg knekte, reiv fengdi utor gapet hans.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
Eg sagde: «I reiret skal eg døy, med dagar talrike som sand.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
Til roti mi skal vatnet trengja, dogg bu ved natt på greini mi;
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
mi æra held seg frisk hjå meg, bogen vert ny handi mi.»
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Dei høyrde ventande på meg, og lydde stilt på rådi mi.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Og ikkje la dei mot mitt ord, min tale draup ned yver deim.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
På meg dei bia som på regn, ja, som vårregn opna munnen.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Eg smilte til mismodige, mitt andlit fekk dei ikkje myrkt.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Når eg deim vitja, sat eg fremst, sat som ein konge i sin herflokk, lik ein som trøystar syrgjande.

< Yobu 29 >