< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Addidit quoque Iob, assumens parabolam suam, et dixit:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Quis mihi tribuat, ut sim iuxta menses pristinos secundum dies, quibus Deus custodiebat me?
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Quando splendebat lucerna eius super caput meum, et ad lumen eius ambulabam in tenebris?
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Sicut fui in diebus adolescentiæ meæ, quando secreto Deus erat in tabernaculo meo?
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
Quando erat Omnipotens mecum: et in circuitu meo pueri mei?
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
Quando lavabam pedes meos butyro, et petra fundebat mihi rivos olei?
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Quando procedebam ad portam civitatis, et in platea parabant cathedram mihi?
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Videbant me iuvenes, et abscondebantur: et senes assurgentes stabant.
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Principes cessabant loqui, et digitum superponebant ori suo.
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
Vocem suam cohibebant duces, et lingua eorum gutturi suo adhærebat.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
Auris audiens beatificabat me, et oculus videns testimonium reddebat mihi.
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Eo quod liberassem pauperem vociferantem, et pupillum, cui non esset adiutor.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
Benedictio perituri super me veniebat, et cor viduæ consolatus sum.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Iustitia indutus sum: et vestivi me, sicut vestimento et diademate, iudicio meo.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Oculus fui cæco, et pes claudo.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Pater eram pauperum: et causam quam nesciebam, diligentissime investigabam.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
Conterebam molas iniqui, et de dentibus illius auferebam prædam.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
Dicebamque: In nidulo meo moriar, et sicut palma multiplicabo dies.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
Radix mea aperta est secus aquas, et ros morabitur in messione mea.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
Gloria mea semper innovabitur, et arcus meus in manu mea instaurabitur.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Qui me audiebant, expectabant sententiam, et intenti tacebant ad consilium meum.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Verbis meis addere nihil audebant, et super illos stillabat eloquium meum.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
Expectabant me sicut pluviam, et os suum aperiebant quasi ad imbrem serotinum.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Siquando ridebam ad eos, non credebant, et lux vultus mei non cadebat in terram.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Si voluissem ire ad eos, sedebam primus: cumque sederem quasi rex, circumstante exercitu, eram tamen mœrentium consolator.

< Yobu 29 >