< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
És továbbá előadta Jób a példázatát és mondta:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Vajha úgy volnék, mint a múltnak hónapjaiban, mint a napokban, mikor Isten megőrzött engem;
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
mikor ragyogott fejem fölött a mécsese s világosságánál sötétben jártam!
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Mint a hogy voltam férfikorom napjaiban, midőn Isten meghittsége volt sátorom felett;
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
midőn még velem volt a Mindenható, körülöttem gyermekeim;
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
midőn lépteim tejfölben fürödtek; s a szikla ontott mellettem olajpatakokat.
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Midőn a kapuhoz mentem a városba, a piaczon választottam ülőhelyemet:
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
megláttak ifjak s elbújtak, aggastyánok fölkeltek, megállottak;
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
vezérek visszatartották beszédjöket és kezüket tették szájukra;
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
előkelőknek hangja elbújt és nyelvök inyökhöz tapadt.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
Mert fül, mely hallott, boldognak mondott engem és szem, mely látott, tanúskodott mellettem.
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Mert megmentettem a szegényt, ki esedezett, és az árvát, kinek nem volt segítője.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
Bujdosónak áldása reám szállt és özvegynek szívét ujjongtattam.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Igazságot öltöttem fel s az felöltött engem, mint köpeny és süveg volt jogosságom.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Szeme voltam a vaknak és lába én a sántának;
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
apjuk én a szűkölködőknek, és annak, kit nem ismertem, pörét átkutattam.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
Összetörtem a jogtalannak zápfogait, és fogai közül vetettem ki a ragadmányt.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
Mondtam: fészkemmel együtt fogok kimúlni s mint a főnix sokasítom napjaimat;
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
gyökerem nyitva van a víznek, és harmat időz gallyamon;
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
dicsőségem szinte új nálam s íjam a kezemben megifjodik.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Rám hallgattak és várakoztak és csendben figyeltek tanácsomra.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Szavam után nem szóltak többet, rájuk cseppegett beszédem;
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
s mint esőre várakoztak: reám, és szájukat tátották tavaszi esőre.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Mosolyogtam rájuk, nem hitték; de arczom világosságát nem sötétítették el.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Választottam útjokat s fejtől ültem s ott időztem, mint király a csapatban mint a ki gyászolókat vigasztal.

< Yobu 29 >