< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
And Job again took up his measure, and said,
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Oh that it were with me as in the months of old, as in the days, when, GOD, used to watch over me;
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
When his lamp shone over my head, by whose light, I could go through darkness;
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
As I was, in the days of my prime, when, the intimacy of GOD, was over my tent;
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
While yet the Almighty was with me, round about me, were my young men;
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
When my steps were bathed in milk, and, the rock, poured out beside me, rivulets of oil:
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
When I went out to the gate unto the city, in the open place, made ready my seat,
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Young men saw me, and hid themselves, and, the aged, arose—they stood;
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Rulers, restrained speech, and, a hand, laid they on their mouth;
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
The voice of nobles, was hushed, and their tongue to their palate, did cleave;
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
When, the ear, heard, then it pronounced me happy, When, the eye, saw, then it bare me witness;
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Because I used to deliver the oppressed who was crying out for aid, the fatherless also, and him that had no helper;
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
The blessing of him that was ready to perish, upon me was wont to descend, and, the heart of the widow, caused I to sing for joy;
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Righteousness, I put on, and it clothed me, Like a robe and turban, was my, justice;
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Eyes, became I to the, blind, and, feet to the lame, was, I!
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
A father, was, I, to the needy, and, as for the cause which I knew not, I used to search it out;
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
And I shivered the fangs of the perverse, —and, out of his teeth, I tare the prey.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
Then said I, Like a stem, shall I grow old, yea, as the sand, shall I multiply days:
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
My root, is laid open to the waters, and, the dew, shall lodge for the night in my boughs;
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
Mine honour, shall be young again with me, and, my bow, in my hand, be renewed.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
To me, men hearkened, and waited, and kept silence for my counsel;
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
After I had spoken, they spake not again, and, upon them, used my speech to drop;
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
And they waited, as for rain, for me, and, their mouths, they opened wide for the spring-rain;
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
I laughed at them—they lost confidence, and, the light of my countenance, they suffered not to fail;
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
I chose out their way, and sat chief, —and abode, as king, in an army, as one who, to mourners, giveth comfort.

< Yobu 29 >