< Yobu 29 >
1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Ještě dále Job vedl řeč svou, a řekl:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Ó bych byl jako za časů předešlých, za dnů, v nichž mne Bůh zachovával,
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Dokudž svítil svící svou nad hlavou mou, při jehož světle chodíval jsem v temnostech,
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Tak jako jsem byl za dnů mladosti své, dokudž přívětivost Boží byla v stanu mém,
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
Dokudž ještě Všemohoucí byl se mnou, a všudy vůkol mne dítky mé,
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
Když šlepěje mé máslem oplývaly, a skála vylévala mi prameny oleje,
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Když jsem vycházel k bráně skrze město, a na ulici strojíval sobě stolici svou.
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Jakž mne spatřovali mládenci, skrývali se, starci pak povstávali a stáli.
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Knížata choulili se v řečech, anobrž ruku kladli na ústa svá.
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
Hlas vývod se tratil, a jazyk jejich lnul k dásním jejich.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
Nebo ucho slyše, blahoslavilo mne, a oko vida, posvědčovalo mi,
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Že vysvobozuji chudého volajícího, a sirotka, i toho, kterýž nemá spomocníka.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
Požehnání hynoucího přicházelo na mne, a srdce vdovy k plésání jsem vzbuzoval.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
V spravedlnost jsem se obláčel, a ona ozdobovala mne; jako plášť a koruna byl soud můj.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Místo očí býval jsem slepému, a místo noh kulhavému.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Byl jsem otcem nuzných, a na při, jíž jsem nebyl povědom, vyptával jsem se.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
A tak vylamoval jsem třenovní zuby nešlechetníka, a z zubů jeho vyrážel jsem loupež.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
A protož jsem říkal: V hnízdě svém umru, a jako písek rozmnožím dny.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
Kořen můj rozloží se při vodách, a rosa nocovati bude na ratolestech mých.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
Sláva má mladnouti bude při mně, a lučiště mé v ruce mé obnovovati se.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Poslouchajíce, čekali na mne, a přestávali na radě mé.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Po slovu mém nic neměnili, tak na ně dštila řeč má.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
Nebo očekávali mne jako deště, a ústa svá otvírali jako k přívalu žádostivému.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Žertoval-li jsem s nimi, nevěřili; pročež u vážnosti mne míti neoblevovali.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Přišel-li jsem kdy k nim, sedal jsem na předním místě, a tak bydlil jsem jako král v vojště, když smutných potěšuje.