< Yobu 29 >
1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Yoube da bu amane sia: i,
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
Gode da musa: na esalusu noga: le ouligi. Na da bu agoane esalumu da defea galu.
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Amo esoga, Gode da na mae fisili, ani ahoasu. Na da gasi ganodini ahoabeba: le, E da nama hadigi iasu.
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Amo esoga na da bagade gaguiwane ba: i. Gode da nama dogolegeiba: le, E da na diasu amola sosogo fi gaga: i.
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
Gode Bagadedafa da ani esalu. Amola na mano huluane hahawane nini dafulili lelefulu.
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
Na bulamagau amola goudi, ilia da dodo maga: me bagade i. Amola na olife ifa ilia da igi galoase osobo da: iya noga: le heda: i.
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Na moilai bai bagade asigilai dunu da sia: sa: imusa: gilisilaloba, na amola da ilima gilisi.
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Ayeligi dunu da na ba: le, gasigasu. Amola da: i hamoi dunu da nama yosia: musa: , wa: legadosu.
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Dunu fi ouligisu dunu da naba: le sia: ouiya: su.
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
Mimogodafa dunu da ouiya: le esalebe ba: su.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
Dunu huluane da na hou ba: beba: le, o enoga amo hou nababeba: le, ilia da na hou amoma nodone sia: i.
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Hame gagui dunu da digini wele sia: beba: le, na da ili fidisu. Na da guluba: mano amo da fidisu dunu hamedafa gala, ili fidi.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
Dunu amo da da: i dioi bagadedafa nabi, ilia da nama nodosu. Amola uda didalo gaga: iwane esaloma: ne, na fidisu.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
Na da eso huluane moloidafa hou fawane hamonanu.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Na da fedege agoane, si dofoi dunu ilia si agoai galusu, amola emo gasuga: igi dunu ilia emo agoai galusu.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Na da hame gagui dunu ilia eda agoai galusu. Amola ga fi da bidi hamosu ba: loba, na da ilimagai galusu.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
Na da nimi bagade dodona: gi dunu ilia gasa wadela: lesi. Amola dunu amo da iliba: le se nabi, amo gaga: i.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
Na da ode bagohame esalumu, amola hahawane na diasuga bogomu dawa: i galu.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
Na da ifa amo ea difi da eso huluane hano defele naha, amola ea amoda amola lubi da eso huluane oubi baeyaga nanegasa, amo defele ba: su.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
Dunu huluane da na houba: le, nodonanusu. Na gasa da hamedafa dafamu agoai ba: su.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Na da fada: i sia: sea, eno dunu da ouiya: lewane nabasu. Ilia da na sia: dawa: iwane nabasu.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Na da sia: dagoloba, ilia eno sia: mu hamedei ba: su. Na sia: da gibu ea dabe agoai ba: su.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
Ifabi ouligisu dunu da woufo oubi gibu yosia: be, amo defele, dunu huluane da na sia: hahawane nabasu.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Ilia da dafawane hamoma: beyale dawa: su fisi dagoi galea, na da ilia dogo denesima: ne, ilima ohomogisu.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Na da ilima ouligisu hou hamone, ilegesu hamosu. Hina bagade da ea dadi gagui wa: i gegemusa: oule ahoabe defele, na da ili bisili oule ahoasu. Amola ilia da heawini da: i dione esalea, na da ilia dogo denesinisisu.