< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Есть бо сребру место, отюнудуже и бывает, и место злату, отюнудуже очищается.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Железо бо из земли раждается, медь же равно камению сечется.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
Чин положи тме, и вся концы сам испытует, камык тмы и сень смерти.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
Пресечение потока от праха: забывающии же путь правый изнемогоша, от человек подвигошася.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
Есть земля, из неяже изыдет хлеб: под нею обратися яко огнь.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
Место сапфира камение ея, и персть злато ему.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
Стезя, не позна ея птица, и не узре ю око супово,
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
и не ходиша по ней сынове величавых, и не прейде по ней лев.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
На несекоме камени простре руку свою, преврати же из корения горы:
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
бреги рек расторже, всякое же честное виде око мое:
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
глубины же рек откры и показа силу свою на свет.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Премудрость же откуду обретеся? И кое место есть ведения?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Не весть человек пути ея, ниже обретеся в человецех.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
Бездна рече: несть во мне: и море рече: несть со мною.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
Не дастся сокровище за ню, и не извесится сребро на изменение ея,
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
и не сравнится со златом Софирским, со ониксом честным и сапфиром:
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
не равно будет ей злато и кристаль, и изменение ея сосуди злати.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
Превысокая и бисерие не помянутся, и притяжи премудрость паче внутреннейших:
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
не уравнится ей топазий Ефиопский, со златом чистым не сравнится.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Премудрость же откуду обретеся? И кое место есть разуму?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Утаися от всякаго человека, и от птиц небесных скрыся.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Пагуба и смерть рекосте: слышахом ея славу.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
Бог благо позна ея путь: Сам бо весть место ея.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
Ибо Сам поднебесную всю надзирает, ведый, яже на земли, вся, яже сотвори.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
Ветров вес и воде меру егда сотворил,
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
тако видяй сочте, и путь в сотрясении гласов,
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
тогда виде ю и поведа ю, уготовав изследи
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
и рече человеку: се, благочестие есть премудрость, а еже удалятися от зла есть ведение.

< Yobu 28 >