< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Mać w prawdzie srebro początki żył swoich, a złoto miejsce, kędy bywa pławione.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Żelazo z ziemi biorą, a z kamienia zlewają miedź.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
Celu ciemnościom ułożonego i końca wszystkich rzeczy on dochodzi, i kamieni, które w ciemności i cieniu śmierci leżą.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
Wyleje rzeka z miejsca swojego, tak, iż jej nikt przebyć nie może, bywa jednak zahamowana przemysłem nędznego człowieka, i odchodzi.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
Z ziemi wychodzi chleb, chociaż pod nią coś różnego, podobnego ogniowi.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
W niektórych miejscach jest kamień Safir, i piasek złoty;
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
A tej ścieszki ani ptak nie wie, ani jej widzało oko sępie.
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
Nie depczą po niej zwierzęta srogie, ani lew przeszedł przez nię.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
Na krzemień ściągnął rękę swoję, wywrócił góry z korzenia;
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
Z skał wywodzi strumienie, a każdą rzecz kosztowną widzi oko jego.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
Wylewać się rzekom nie dopuszcza, a rzeczy skryte wywodzi na jaśnię.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Ale mądrość gdzież może być znaleziona? a kędy jest miejsce roztropności?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Nie wie człowiek śmiertelny ceny jej, ani bywa znaleziona w ziemi żyjących.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
Przepaść mówi: Niemasz jej we mnie; i morze też powiada: Niemasz jej u mnie.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
Nie dawają szczerego złota za nię; ani odważają srebra, za odmianę jej.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
Nie może być oszacowana za złoto Ofir, ani za Onychyn drogi, ani za Safir.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Nie porówna z nią złoto, ani kryształ, ani odmiana jej może być za klejnot złota szczerego.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
Koralów i pereł nie wspomina, bo nabycie mądrości kosztowniejsze jest nad perły.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
Nie zrówna z nią i szmaragd z ziemi etyjopskiej; ani za złoto najczystsze szacowana być może.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Skądże tedy mądrość pochodzi? albo gdzie jest miejsce rozumu?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Gdyż zakryta jest od oczu wszystkich żyjących, i przed ptastwem niebieskim zatajona jest.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Zginienie i śmierć rzekły: Uszyma swemi słyszałyśmy sławę jej.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
Bóg sam rozumie drogę jej, a on wie miejsce jej.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
Bo on na kończyny ziemi patrzy, a wszystko, co jest pod niebem, widzi.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
Wiatrom uczynił wagę, a wody odważył pod miarą.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
On też prawo dżdżom postanowił, a drogę błyskawicom gromów.
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
W ten czas ją widział, i głosił ją: zgotował ją, i doszedł jej.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
Ale człowiekowi rzekł: Oto bojaźń Pańska jest mądrością, a warować się złego, jest rozumem.

< Yobu 28 >