< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Habet argentum, venarum suarum principia: et auro locus est, in quo conflatur.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Ferrum de terra tollitur: et lapis solutus calore, in aes vertitur.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
Tempus posuit tenebris, et universorum finem ipse considerat, lapidem quoque caliginis, et umbram mortis.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
Dividit torrens a populo peregrinante, eos, quos oblitus est pes egentis hominis, et invios.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
Terra, de qua oriebatur panis in loco suo, igni subversa est.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
Locus sapphiri lapides eius, et glebae illius aurum.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
Semitam ignoravit avis, nec intuitus est eam oculus vulturis.
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
Non calcaverunt eam filii institorum, nec pertransivit per eam leaena.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
Ad silicem extendit manum suam, subvertit a radicibus montes.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
In petris rivos excidit, et omne pretiosum vidit oculus eius.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
Profunda quoque fluviorum scrutatus est, et abscondita in lucem produxit.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Sapientia vero ubi invenitur? et quis est locus intelligentiae?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Nescit homo pretium eius, nec invenitur in terra suaviter viventium.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
Abyssus dicit: Non est in me: et mare loquitur: Non est mecum.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
Non dabitur aurum obrizum pro ea, nec appendetur argentum in commutatione eius.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
Non conferetur tinctis Indiae coloribus, nec lapidi sardonycho pretiosissimo, vel sapphiro.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Non adaequabitur ei aurum vel vitrum, nec commutabuntur pro ea vasa auri:
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
Excelsa et eminentia non memorabuntur comparatione eius: trahitur autem sapientia de occultis.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
Non adaequabitur ei topazius de Aethiopia, nec tincturae mundissimae componetur.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Unde ergo sapientia venit? et quis est locus intelligentiae?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Abscondita est ab oculis omnium viventium, volucres quoque caeli latet.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Perditio et mors dixerunt: Auribus nostris audivimus famam eius.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
Deus intelligit viam eius, et ipse novit locum illius.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
Ipse enim fines mundi intuetur: et omnia, quae sub caelo sunt, respicit.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
Qui fecit ventis pondus, et aquas appendit in mensura.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
Quando ponebat pluviis legem, et viam procellis sonantibus:
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
Tunc vidit illam, et enarravit, et praeparavit, et investigavit.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
Et dixit homini: Ecce timor Domini, ipsa est sapientia: et recedere a malo, intelligentia.

< Yobu 28 >