< Yobu 28 >
1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
L’argent a des sources de ses veines, et il y a pour l’or un lieu où il est mis en fusion.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Le fer est tiré de la terre, et une pierre dissoute par la chaleur est changée en airain.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
Il a posé un temps déterminé aux ténèbres, et il considère lui-même la fin de toutes choses, aussi bien qu’une pierre cachée dans l’obscurité, et que l’ombre de la mort.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
Un torrent sépare d’un peuple étranger ceux que le pied de l’homme indigent a oubliés, et qui sont inaccessibles.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
Une terre d’où naissait du pain, a été bouleversée en son lieu par le feu.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
Ses pierres sont le lieu du saphir, et ses glèbes sont de l’or.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
L’oiseau en a ignoré le sentier, et l’œil d’un vautour ne l’a pas regardé.
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
Les fils des marchands ne l’ont pas foulé, et la lionne ne l’a pas traversé.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
Il a étendu sa main contre des rochers, il a renversé des montagnes jusqu’à leurs racines.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
Il a creusé des ruisseaux dans les pierres, et son œil a vu tout ce qu’il y a de précieux.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
Il a scruté aussi les profondeurs des fleuves, et il a produit à la lumière des choses cachées.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Mais la sagesse, où se trouve-t-elle? Et quel est le lieu de l’intelligence?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
L’homme n’en connaît pas le prix, et elle ne se trouve pas dans la terre de ceux qui vivent dans les délices.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
L’abîme dit: Elle n’est pas en moi; la mer dit aussi; Elle n’est pas avec moi.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
On ne la donnera pas pour l’or le plus affiné, et on ne l’échangera pas contre de l’argent au poids.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
On ne la comparera point aux tissus colorés de l’Inde, ni à la sardoine la plus précieuse ou au saphir.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
On ne lui égalera point l’or ou le verre, et on ne l’échangera point contre des vases d’or.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
Ce qu’il y a de plus grand et de plus élevé ne sera pas même nommé auprès d’elle, mais la sagesse a une origine secrète.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
On ne lui égalera pas la topaze de l’Ethiopie, et on ne la comparera pas aux teintures les plus éclatantes.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
D’où vient donc la sagesse, et quel est le lieu de l’intelligence?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Elle est cachée aux yeux de tous les vivants, elle est inconnue aux oiseaux mêmes du ciel.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
La perdition et la mort ont dit: Nous avons ouï son nom de nos oreilles.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
C’est Dieu qui comprend sa voie, et c’est lui qui connaît son lieu.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
Car c’est lui qui observe les extrémités du monde, et qui considère tout ce qui est sous le ciel.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
C’est lui qui a fait un poids aux vents, et qui a pesé les eaux avec une mesure.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
Quand il imposait aux pluies une loi, et une voix aux tempêtes tonnantes,
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
C’est alors qu’il l’a vue, qu’il l’a proclamée, et qu’il l’a scrutée.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
Et il a dit à l’homme: Voici; la crainte du Seigneur, c’est la sagesse, et s’éloigner du mal, l’intelligence.