< Yobu 28 >
1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Surely there is a mine for silver, a place where they refine gold.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Iron is taken out of the earth; copper is smelted out of the stone.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
A man sets an end to darkness and searches out, to the farthest limit, the stones in obscurity and thick darkness.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
He breaks open a shaft away from where people live, places that are forgotten by anyone's foot. He hangs far away from people; he swings to and fro.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
As for the earth, out of which comes bread, it is turned up below as if by fire.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
Its stones are the place where sapphires are found, and its dust contains gold.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
No bird of prey knows the path to it, nor has the falcon's eye seen it.
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
The proud animals have not walked such a path, nor has the fierce lion passed there.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
A man lays his hand on the flinty rock; he overturns mountains by their roots.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
He cuts out channels among the rocks; his eye sees every valuable thing there.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
He ties up the streams so they do not run; what is hidden there he brings out to the light.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Where will wisdom be found? Where is the place of understanding?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Man does not know its price; neither is it found in the land of the living.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
The deep waters under the earth say, 'It is not in me'; the sea says, 'It is not with me.'
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
It cannot be gotten for gold; neither can silver be weighed as its price.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
It cannot be valued with the gold of Ophir, with precious onyx or sapphire.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Gold and crystal cannot equal it in worth; neither can it be exchanged for jewels of fine gold.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
No mention is worth making of coral or jasper; indeed, the price of wisdom is more than rubies.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
The topaz of Cush does not equal it; neither can it be valued in terms of pure gold.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
From where, then, comes wisdom? Where is the place of understanding?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Wisdom is hidden from the eyes of all living things and is kept hidden from the birds of the heavens.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Destruction and Death say, 'We have heard just a rumor about it with our ears.'
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
God understands the way to it; he knows its place.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
For he looks to the very ends of the earth and sees under all the heavens.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
He made the force of the wind and parceled out the waters by measure.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
He made a decree for the rain and a path for the thunder.
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
Then he saw wisdom and announced it; he established it, indeed, and he examined it.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
To people he said, 'See, the fear of the Lord—that is wisdom; to depart from evil is understanding.'”