< Yobu 28 >
1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
For truly there is a source for the silver, and a place for the gold which men refine.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Iron is taken out of the dust, and the stone is melted into copper.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
An end doth he set to darkness, and the very utmost limit doth he search out, the stones of darkness, and of the shadow of death.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
He breaketh a channel far from the inhabited place; those of unsteady foot, the poorest of men move [there about].
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
The earth, out of which cometh forth bread, is under its surface turned up as it were with fire.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
Her stones are the place whence the sapphire cometh; and golden dust is also there;
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
[On the] path which no bird of prey knoweth, and which the vulture's eye hath not surveyed;
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
[Which] ravenous beasts have never trodden, over which the lion hath never passed.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
To the flinty rock he stretcheth forth his hand; he overturneth the mountains from the root.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
Amid rocks he heweth out canals: and every precious thing doth his eye behold.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
The various droppings of water he uniteth into streams, and what is hidden he bringeth forth to light.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
But wisdom—where shall she he found? and where is the place of understanding?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Man knoweth not her value: and she is not to be found in the land of the living.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
The deep saith, Not in me is she: and the sea saith, She is not with me.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
No fine gold can be given in lieu of her, and silver cannot be weighed out as her price.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
She cannot be valued with the gold of Ophir, with the precious onyx, or the sapphire.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
She cannot be estimated after gold and glass; and not in exchange for her [can] vessels of refined gold [be taken.]
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
Coral and crystal will not be thought of; and the value of wisdom is above pearls.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
She cannot be estimated after the topaz of Ethiopia, nor can she be valued with pure gold.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
But wisdom—whence cometh she? and where is the place of understanding?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Yea, she is hidden from the eyes of all living, and from the fowls of the heavens is she concealed.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Perdition and death say, With our ears have we heard a report of her.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
God [alone] understandeth her way, and he knoweth her place;
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
For he looketh to the ends of the earth, [whatever is] under the whole heaven doth he see.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
When he imparted weight unto the wind; and [when] the waters he established by measure;
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
When he made a law for the rain, and a way for the lightning of [his] thunders;
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
Then did he see her, and make her known; he established her, and also searched her out.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
And he said unto man, Behold, the fear of the Lord, that is wisdom; and to eschew evil is understanding.