< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
For there is a mine for silver, and a place for gold which they refine.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Iron is taken out of the dust, and brass is molten out of the stone.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
Man setteth an end to darkness, and searcheth out to the furthest bound the stones of thick darkness and of the shadow of death.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
He breaketh open a shaft away from where men sojourn; they are forgotten of the foot that passeth by; they hang afar from men, they swing to and fro.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
As for the earth, out of it cometh bread, and underneath it is turned up as it were by fire.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
The stones thereof are the place of sapphires, and it hath dust of gold.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
That path no bird of prey knoweth, neither hath the falcon's eye seen it;
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
The proud beasts have not trodden it, nor hath the lion passed thereby.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
He putteth forth his hand upon the flinty rock; He overturneth the mountains by the roots.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
He cutteth out channels among the rocks; and his eye seeth every precious thing.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
He bindeth the streams that they trickle not; and the thing that is hid bringeth he forth to light.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
But wisdom, where shall it be found? And where is the place of understanding?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Man knoweth not the price thereof; neither is it found in the land of the living.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
The deep saith: 'It is not in me'; and the sea saith: 'It is not with me.'
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
It cannot be gotten for gold, neither shall silver be weighed for the price thereof.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
It cannot be valued with the gold of Ophir, with the precious onyx, or the sapphire.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Gold and glass cannot equal it; neither shall the exchange thereof be vessels of fine gold.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
No mention shall be made of coral or of crystal; yea, the price of wisdom is above rubies.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
The topaz of Ethiopia shall not equal it, neither shall it be valued with pure gold.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Whence then cometh wisdom? And where is the place of understanding?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Seeing it is hid from the eyes of all living, and kept close from the fowls of the air.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Destruction and Death say: 'We have heard a rumor thereof with our ears.'
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
God understandeth the way thereof, and He knoweth the place thereof.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
For He looketh to the ends of the earth, and seeth under the whole heaven;
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
When He maketh a weight for the wind, and meteth out the waters by measure.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
When He made a decree for the rain, and a way for the storm of thunders;
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
Then did He see it, and declare it; He established it, yea, and searched it out.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
And unto man He said: 'Behold, the fear of the Lord, that is wisdom; and to depart from evil is understanding.'

< Yobu 28 >